< Hiob 8 >

1 Na Suhini Bildad buae se:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Wobɛkɔ so aka saa nsɛm yi akosi da bɛn? Wo nsɛm yɛ mframa huhuw.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Onyankopɔn kyea atɛntrenee ana? Otumfo kyea nea ɛteɛ ana?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Bere a wo mma yɛɛ bɔne tiaa no no, ogyaw wɔn maa wɔn bɔne so akatua.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Nanso sɛ wode wʼani bɛto Onyankopɔn so na woabɔ Otumfo no mpae,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 sɛ woyɛ kronkron, na woteɛ a, wo nti, ɔbɛma ne ho so mprempren na wama wo asi wo dedaw mu.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Wo mfiase bɛyɛ nkakrankakra na daakye woanya ama abu so.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 “Bisa awo ntoatoaso a atwa mu no, na hwehwɛ nea wɔn agyanom hui,
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 na wɔwoo yɛn nkyɛe na yennim hwee, yɛn nna wɔ asase yi so te sɛ sunsuma.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Wɔrenkyerɛkyerɛ wo na wɔrenka nkyerɛ wo ana? Wɔremfi wɔn ntease mu nka nsɛm bi ana?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 So paparɔso betumi anyin akɔ soro wɔ baabi a ɛnyɛ ɔwora? Demmire betumi afifi baabi a nsu nni ana?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Bere a ɛrenyin a wontwae no, ɛhyew ntɛm so sen sare.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Saa na wɔn a wɔn werɛ fi Onyankopɔn no awiei te; saa ara na wɔn a wonni nyamesu no anidaso nkosi hwee.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Biribiara a nʼani da so no nni ahoɔden; nea ɔde ne ho to so no yɛ ananse ntontan.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Otweri ne ntontan, nanso ɛtetew; oso mu dennen, nanso ɛnyɛ yie.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Ɔte sɛ afifide a wogugu so nsu yiye a esi owia mu, ɛtrɛtrɛw ne mman mu wɔ turo no so;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Ne ntin nyin fa abotan ho, na ɛhwehwɛ ɔkwan kɔ abo mu.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Nanso sɛ wotu fi ne sibea a, saa beae no nnim no bio na ɛka se, ‘Minhuu wo da.’
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ampa ara ne nkwa twa mu, na afifide foforo nyin asase no so.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 “Ampa ara Onyankopɔn mpo onipa a ne ho nni asɛm na ɔnhyɛ amumɔyɛfo nsa mu den.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Ɔbɛma woaserew bio, na wode ahosɛpɛw ateɛteɛ mu.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Wɔde aniwu befura wɔn a wɔtan wo, na amumɔyɛfo ntamadan bɛsɛe.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Hiob 8 >