< Romalilar 8 >

1 Böylece Mesih İsa'ya ait olanlara artık hiçbir mahkûmiyet yoktur.
Choncho, tsopano amene ali mwa Khristu Yesu alibe mlandu owatsutsa
2 Çünkü yaşam veren Ruh'un yasası, Mesih İsa sayesinde beni günahın ve ölümün yasasından özgür kıldı.
chifukwa mwa Khristu Yesu, lamulo la Mzimu Woyera amene amapereka moyo, lawamasula ku lamulo la tchimo ndi la imfa.
3 İnsan benliğinden ötürü güçsüz olan Kutsal Yasa'nın yapamadığını Tanrı yaptı. Öz Oğlu'nu günahlı insan benzerliğinde günah sunusu olarak gönderip günahı insan benliğinde yargıladı.
Pakuti zimene Malamulo sanathe kuzichita, popeza anali ofowoka chifukwa cha khalidwe lathu la uchimo, Mulungu anazichita potumiza Mwana wake mʼchifanizo cha munthu ochimwa kuti akhale nsembe yauchimo. Ndipo Iye anagonjetsa tchimo mʼthupi la munthu,
4 Öyle ki, Yasa'nın gereği, benliğe göre değil, Ruh'a göre yaşayan bizlerde yerine gelsin.
ndi cholinga chakuti chilungamo chofunikira cha lamulo chikwaniritsidwe kwathunthu mwa ife amene sitikhala monga mwachikhalidwe chathu cha uchimo koma mwa Mzimu.
5 Benliğe uyanlar benlikle ilgili, Ruh'a uyanlarsa Ruh'la ilgili işleri düşünürler.
Pakuti anthu amene amakhala monga mwa makhalidwe oyipa a thupi amayika malingaliro awo pa zinthu zathupi. Koma amene amakhala monga mwa Mzimu amayika malingaliro awo pa zinthu za Mzimu.
6 Benliğe dayanan düşünce ölüm, Ruh'a dayanan düşünceyse yaşam ve esenliktir.
Kuyika mtima pa zathupi ndi imfa koma kuyika mtima pa za Mzimu ndi moyo ndi mtendere.
7 Çünkü benliğe dayanan düşünce Tanrı'ya düşmandır; Tanrı'nın Yasası'na boyun eğmez, eğemez de...
Pakuti mtima umene wakhazikika pa zathupi ndi wodana ndi Mulungu. Sunagonjere lamulo la Mulungu ndipo sungathe kutero.
8 Benliğin denetiminde olanlar Tanrı'yı hoşnut edemezler.
Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.
9 Ne var ki, Tanrı'nın Ruhu içinizde yaşıyorsa, benliğin değil, Ruh'un denetimindesiniz. Ama içinde Mesih'in Ruhu olmayan kişi Mesih'in değildir.
Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lauchimo koma ndi Mzimu ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu si wa Khristu.
10 Eğer Mesih içinizdeyse, bedeniniz günah yüzünden ölü olmakla birlikte, aklanmış olduğunuz için ruhunuz diridir.
Ndipo ngati Khristu ali mwa inu, thupi lanu ndi lakufa chifukwa cha uchimo, koma mzimu wanu ndi wamoyo chifukwa cha chilungamo.
11 Mesih İsa'yı ölümden dirilten Tanrı'nın Ruhu içinizde yaşıyorsa, Mesih'i ölümden dirilten Tanrı, içinizde yaşayan Ruhu'yla ölümlü bedenlerinize de yaşam verecektir.
Ndipo ngati Mzimu wa Mulungu amene anaukitsa Yesu kwa akufa akhala mwa inu, Iyeyo amene anaukitsa Khristu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu amene amafa kudzera mwa Mzimu wake amene amakhala mwa inu.
12 Öyleyse kardeşlerim, borçluyuz ama, benliğe göre yaşamak için benliğe borçlu değiliz.
Kotero abale, ife tili ndi zoti tikwaniritse, koma osati za khalidwe lathu lauchimo, kumachita zofuna zake.
13 Çünkü benliğe göre yaşarsanız öleceksiniz; ama bedenin kötü işlerini Ruh'la öldürürseniz yaşayacaksınız.
Pakuti ngati inu mukhala monga mwa khalidwe lauchimo, mudzafa. Koma ngati mwa Mzimu mupha ntchito zoyipa zathupi, mudzakhala ndi moyo.
14 Tanrı'nın Ruhu'yla yönetilenlerin hepsi Tanrı'nın oğullarıdır.
Onse amene amatsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu ndi ana a Mulungu.
15 Çünkü sizi yeniden korkuya sürükleyecek kölelik ruhunu almadınız, oğulluk ruhunu aldınız. Bu ruhla, “Abba, Baba!” diye sesleniriz.
Mzimu amene inu munalandira samakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha, koma Mzimu amakusandutsani ana. Ndipo mwa Iye ife timafuwula kuti, “Abba, Atate.”
16 Ruh'un kendisi, bizim ruhumuzla birlikte, Tanrı'nın çocukları olduğumuza tanıklık eder.
Mzimu mwini amavomerezana ndi mzimu wathu kuti ife ndife ana a Mulungu.
17 Eğer Tanrı'nın çocuklarıysak, aynı zamanda mirasçıyız. Mesih'le birlikte yüceltilmek üzere Mesih'le birlikte acı çekiyorsak, Tanrı'nın mirasçılarıyız, Mesih'le ortak mirasçılarız.
Tsono ngati tili ana ake, ndiye kuti ndife olowa mʼmalo a Mulungu ndi olowa mʼmalo pamodzi ndi Khristu. Ngati ife timva zowawa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye.
18 Kanım şu ki, bu anın acıları, gözümüzün önüne serilecek yücelikle karşılaştırılmaya değmez.
Ine ndiganiza kuti masautso amene tikuwamva nthawi ino, sakufanana ndi ulemerero umene udzaonetsedwa mwa ife.
19 Yaratılış, Tanrı çocuklarının ortaya çıkmasını büyük özlemle bekliyor.
Pakuti chilengedwe chikudikira ndi chiyembekezo kuonetsedwa poyera kwa ana a Mulungu.
20 Çünkü yaratılış amaçsızlığa teslim edildi. Bu da yaratılışın isteğiyle değil, onu amaçsızlığa teslim eden Tanrı'nın isteğiyle oldu. Çünkü yaratılışın, yozlaşmaya köle olmaktan kurtarılıp Tanrı çocuklarının yüce özgürlüğüne kavuşturulması umudu vardı.
Pakuti chilengedwe sichinasankhe kugonjera zopanda pake, koma mwachifuniro cha Iye amene analola kuti chigonjere. Koma chili ndi chiyembekezo
chakuti chidzamasulidwa ku ukapolo wa chivundi ndi kulandiranso ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu.
22 Bütün yaratılışın şu ana dek birlikte inleyip doğum ağrısı çektiğini biliyoruz.
Ife tikudziwa kuti chilengedwe chonse chakhala chikubuwula ndi ululu ngati ululu wa nthawi yobereka mwana mpaka tsopano lino.
23 Yalnız yaratılış değil, biz de –evet Ruh'un turfandasına sahip olan bizler de– evlatlığa alınmayı, yani bedenlerimizin kurtulmasını özlemle bekleyerek içimizden inliyoruz.
Si zokhazo ayi, ngakhale ife tomwe, amene tili ndi zipatso zoyamba za Mzimu, tikubuwulira mʼkati mwathu pomwe tikudikira mwachidwi kusankhidwa kwathu ngati ana, kuwomboledwa kwa matupi athu.
24 Çünkü bu umutla kurtulduk. Ama görülen umut, umut değildir. Gördüğü şeyi kim umut eder?
Pakuti ife tinapulumutsidwa mʼchiyembekezo ichi. Koma chiyembekezo chimene chimaoneka si chiyembekezo ayi. Kodi ndani amene amayembekezera chimene ali nacho kale?
25 Oysa görmediğimize umut bağlarsak, sabırla bekleyebiliriz.
Koma ngati ife tiyembekeza chimene tikanalibe, ndiye kuti tikuyembekeza modekha mtima.
26 Bunun gibi, Ruh da güçsüzlüğümüzde bize yardım eder. Ne için dua etmemiz gerektiğini bilmeyiz, ama Ruh'un kendisi, sözle anlatılamaz iniltilerle bizim için aracılık eder.
Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa.
27 Yürekleri araştıran Tanrı, Ruh'un düşüncesinin ne olduğunu bilir. Çünkü Ruh, Tanrı'nın isteği uyarınca kutsallar için aracılık eder.
Koma Iye amene amasanthula mitima yathu amadziwa maganizo a Mzimu, chifukwa Mzimu amapempherera oyera mtima molingana ndi chifuniro cha Mulungu.
28 Tanrı'nın, kendisini sevenlerle, amacı uyarınca çağrılmış olanlarla birlikte her durumda iyilik için etkin olduğunu biliriz.
Ndipo ife tikudziwa kuti zinthu zonse zimathandizana kuwachitira ubwino amene amakonda Mulungu, amene anayitanidwa monga mwa cholinga chake.
29 Çünkü Tanrı önceden bildiği kişileri Oğlu'nun benzerliğine dönüştürmek üzere önceden belirledi. Öyle ki, Oğul birçok kardeş arasında ilk doğan olsun.
Pakuti amene Mulungu anawadziwiratu, anawasankhiratunso kuti akonzedwe mʼchifanizo cha Mwana wake, kuti Iye akhale Mwana woyamba kubadwa mwa abale ambiri.
30 Tanrı önceden belirlediği kişileri çağırdı, çağırdıklarını akladı ve akladıklarını yüceltti.
Iwo amene anawasankhiratu, anawayitananso. Amene Iye anawayitana anawalungamitsanso ndipo amene anawalungamitsa anawapatsanso ulemerero.
31 Öyleyse buna ne diyelim? Tanrı bizden yanaysa, kim bize karşı olabilir?
Nanga tsono tidzanena chiyani pa izi? Ngati Mulungu ali mbali yathu, adzatitsutsa ife ndani?
32 Öz Oğlu'nu bile esirgemeyip O'nu hepimiz için ölüme teslim eden Tanrı, O'nunla birlikte bize her şeyi bağışlamayacak mı?
Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anamupereka chifukwa cha ife tonse. Iye adzalekeranjinso pamodzi naye kutipatsa ife zinthu zonse mwaulere?
33 Tanrı'nın seçtiklerini kim suçlayacak? Onları aklayan Tanrı'dır.
Ndani amene adzabweretsa mlandu kutsutsa amene Mulungu anawasankha? Ndi Mulungu amene amalungamitsa.
34 Kim suçlu çıkaracak? Ölmüş, üstelik dirilmiş olan Mesih İsa, Tanrı'nın sağındadır ve bizim için aracılık etmektedir.
Ndani amene angatipeze ife olakwa? Palibe. Khristu Yesu amene anafa, kuposera pamenepo, amene anaukitsidwa ndi moyo, amene ali kudzanja lamanja la Mulungu ndiye amene akutipempherera.
35 Mesih'in sevgisinden bizi kim ayırabilir? Sıkıntı mı, elem mi, zulüm mü, açlık mı, çıplaklık mı, tehlike mi, kılıç mı?
Ndani amene adzatilekanitsa ife ndi chikondi cha Khristu? Kodi ndi masautso, kapena zowawa, kapena mazunzo, kapena njala, kapena umaliseche, kapena choopsa, kapena lupanga?
36 Yazılmış olduğu gibi: “Senin uğruna bütün gün öldürülüyoruz, Kasaplık koyun sayılıyoruz.”
Monga kwalembedwa: “Chifukwa cha inu, ife tikuphedwa tsiku lonse: ife tikutengedwa ngati nkhosa zoti zikaphedwe.”
37 Ama bizi sevenin aracılığıyla bu durumların hepsinde galiplerden üstünüz.
Ayi, mu zonsezi ife ndife oposa agonjetsi mwa Iye amene anatikonda.
38 Eminim ki, ne ölüm, ne yaşam, ne melekler, ne yönetimler, ne şimdiki ne gelecek zaman, ne güçler, ne yükseklik, ne derinlik, ne de yaratılmış başka bir şey bizi Rabbimiz Mesih İsa'da olan Tanrı sevgisinden ayırmaya yetecektir.
Pakuti ine ndatsimikiza ndi mtima wonse kuti ngakhale imfa, kapena moyo, ngakhale angelo, kapena ziwanda, ngakhale zinthu zilipo, kapena zili mʼtsogolo, kapena mphamvu zina,
ngakhale kutalika, kapena kuya, kapena chilichonse mʼchilengedwe chonse, sizingathe kutisiyanitsa ndi chikondi cha Mulungu chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

< Romalilar 8 >