< Romalilar 15 >

1 İmanı güçlü olan bizler, kendimizi hoşnut etmeye değil, güçsüzlerin zayıflıklarını yüklenmeye borçluyuz.
Ife amene tili ndi chikhulupiriro champhamvu tiziwalezera mtima anthu ofowoka, ndipo tisamadzikondweretse tokha.
2 Her birimiz komşusunu ruhça geliştirmek için komşusunun iyiliğini gözeterek onu hoşnut etsin.
Aliyense wa ife akondweretse mnzake pomuchitira zabwino zomulimbikitsa.
3 Çünkü Mesih bile kendini hoşnut etmeye çalışmadı. Yazılmış olduğu gibi: “Sana edilen hakaretlere ben uğradım.”
Pakuti ngakhale Khristu sanadzikondweretsa yekha koma, monga kwalembedwa kuti, “Chipongwe cha anthu okunyozani chinagwera Ine.”
4 Önceden ne yazıldıysa, bize öğretmek için, sabırla ve Kutsal Yazılar'ın verdiği cesaretle umudumuz olsun diye yazıldı.
Pakuti zilizonse zimene zinalembedwa kale zinalembedwa kuti zitiphunzitse ife. Malembawo amatilimbikitsa kupirira kuti tikhale ndi chiyembekezo.
5 Sabır ve cesaret kaynağı olan Tanrı'nın, sizleri Mesih İsa'nın isteğine uygun olarak aynı düşüncede birleştirmesini dilerim.
Mulungu amene amapereka kupirira ndi chilimbikitso akupatseni maganizo amodzi pakati panu monga inu mukutsatira Khristu Yesu,
6 Öyle ki, Rabbimiz İsa Mesih'in Tanrısı'nı ve Babası'nı birlik içinde hep bir ağızdan yüceltesiniz.
kotero kuti ndi mtima umodzi ndi movomerezana mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.
7 Bu nedenle, Mesih sizi kabul ettiği gibi, Tanrı'nın yüceliği için birbirinizi kabul edin.
Tsopano landiranani wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, ndi cholinga choti Mulungu alemekezeke.
8 Çünkü diyorum ki Mesih, Tanrı'nın güvenilir olduğunu göstermek için Yahudiler'in hizmetkârı oldu. Öyle ki, atalarımıza verilen sözler doğrulansın ve öteki uluslar merhameti için Tanrı'yı yüceltsin. Yazılmış olduğu gibi: “Bunun için uluslar arasında sana şükredeceğim, Adını ilahilerle öveceğim.”
Chifukwa kunena zoona, Khristu wasanduka mtumiki wa Ayuda, kuonetsa kuti Mulungu ndi wokhulupirika pa malonjezo amene anachita kwa makolo awo
9
kuti a mitundu ina atamande Mulungu chifukwa cha chifundo chake. Monga kwalembedwa kuti, “Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa a mitundu; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”
10 Yine deniyor ki, “Ey uluslar, O'nun halkıyla birlikte sevinin!” Ve, “Ey bütün uluslar, Rab'be övgüler sunun! Ey bütün halklar, O'nu yüceltin!”
Akutinso, “Kondwerani inu anthu a mitundu ina pamodzi ndi anthu ake.”
Ndipo akutinso, “Tamandani Ambuye, inu nonse a mitundu ina, ndi kuyimba zotamanda Iye, inu anthu onse.”
12 Yeşaya da şöyle diyor: “İşay'ın Kökü ortaya çıkacak, Uluslara egemen olmak üzere yükselecek. Uluslar O'na umut bağlayacak.”
Ndiponso Yesaya akuti, “Muzu wa Yese udzaphuka, wina amene adzauka kulamulira anthu a mitundu ina; mwa Iye mudzakhala chiyembekezo cha a mitundu ina.”
13 Umut kaynağı olan Tanrı, Kutsal Ruh'un gücüyle umutla dolup taşmanız için iman yaşamınızda sizleri tam bir sevinç ve esenlikle doldursun.
Mulungu amene amatipatsa chiyembekezo adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pamene mukumudalira Iye, kuti chiyembekezo chanu chisefukire mwamphamvu ya Mzimu Woyera.
14 Size gelince, kardeşlerim, iyilikle dolu, her bilgiyle donanmış olduğunuzdan ben eminim. Ayrıca, birbirinize öğüt verebilecek durumdasınız.
Abale anga, ine mwini ndikutsimikiza kuti inuyo ndinu abwino, odzaza ndi chidziwitso ndi okhoza kulangizana wina ndi mnzake.
15 Yine de Tanrı'nın bana bağışladığı lütufla bazı noktaları yeniden anımsatmak için size yazma cesaretini gösterdim.
Ine ndakulemberani inu molimba mtima pa fundo zina, kukhala ngati kukukumbutsaninso za zimenezo, chifukwa cha chisomo chimene Mulungu anandipatsa ine
16 Ben Tanrı'nın lütfuyla uluslar yararına Mesih İsa'nın hizmetkârı oldum. Tanrı'nın Müjdesi'ni bir kâhin olarak yaymaktayım. Öyle ki uluslar, Kutsal Ruh'la kutsal kılınarak Tanrı'yı hoşnut eden bir sunu olsun.
kukhala mtumiki wa Khristu Yesu wa a mitundu ina ndi udindo wa wansembe, kulalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu, kuti a mitundu ina akhale nsembe yolandiridwa kwa Mulungu, yopatsidwa ndi Mzimu Woyera.
17 Bunun için Mesih İsa'ya ait biri olarak Tanrı'ya verdiğim hizmetle övünebilirim.
Choncho, ine ndikunyadira mwa Khristu Yesu potumikira Mulungu wanga.
18 Ulusların söz dinlemesi için Mesih'in benim aracılığımla, sözle ve eylemle, mucizeler ve harikalar yaratan güçle, Kutsal Ruh'un gücüyle yaptıklarından başka şeyden söz etmeye cesaret edemem. Yeruşalim'den başlayıp İllirikum bölgesine kadar dolaşarak Mesih'in Müjdesi'ni eksiksiz duyurdum.
Ine sindidzayesera kuyankhula za kanthu kalikonse koma zimene Khristu wazichita kudzera mwa ine zotsogolera a mitundu ina kuti amvere Mulungu mwa zimene ndinanena ndi kuzichita
mwamphamvu ya zizindikiro ndi zodabwitsa kudzera mwamphamvu ya Mzimu Woyera. Choncho kuchokera ku Yerusalemu ndi kuzungulira ku Iluriko, ine ndalalikira kwathunthu Uthenga Wabwino wa Khristu.
20 Bir başkasının attığı temel üzerine inşa etmemek için Müjde'yi Mesih'in adının duyulmadığı yerlerde yaymayı amaç edindim.
Chakhala chilakolako changa nthawi zonse kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kumene Khristu sadziwika, kuti ine ndisamange pa maziko a wina wake.
21 Yazılmış olduğu gibi: “O'ndan habersiz olanlar görecekler. Duymamış olanlar anlayacaklar.”
Koma monga kwalembedwa kuti, “Iwo amene sanawuzidwe za Iye adzaona, ndi iwo amene sanamve adzazindikira.”
22 İşte bu yüzden yanınıza gelmem kaç kez engellendi.
Ichi nʼchifukwa chake ine ndakhala ndikuletsedwa kawirikawiri kubwera kwa inu.
23 Şimdiyse bu yörelerde artık yapacağım bir şey kalmadığından, yıllardır da yanınıza gelmeyi arzuladığımdan, İspanya'ya giderken size uğrarım. Yol üzerinde sizi görüp bir süre arkadaşlığınıza doyduktan sonra beni oraya uğurlayacağınızı umarım.
Koma tsopano popeza kulibenso malo anga woti ndigwire ntchito mʼmadera awa, ndakhala ndikufuna kukuonani kwa zaka zambiri.
Ine ndikukonza kuti nditero pamene ndipita ku Spaniya. Ine ndikuyembekeza kudzakuchezerani pamene ndikudutsa ndi kuti inu mudzathandize popitiriza ulendo wanga, nditasangalala ndi kukhala nanu kwa kanthawi.
25 Ama şimdi kutsallara bir hizmet için Yeruşalim'e gidiyorum.
Koma tsopano, ine ndili pa ulendo wopita ku Yerusalemu potumikira oyera mtima akumeneko.
26 Çünkü Makedonya ve Ahaya'da bulunanlar, Yeruşalim'deki kutsallar arasında yoksul olanlar için yardım toplamayı uygun gördüler.
Pakuti kunakomera a ku Makedoniya ndi a ku Akaya kupereka thandizo kwa osauka pakati pa oyera mtima mu Yerusalemu.
27 Evet, uygun gördüler. Gerçekte onlara yardım borçlular. Uluslar, onların ruhsal bereketlerine ortak olduklarına göre, maddesel bereketlerle onlara hizmet etmeye borçlular.
Iwo chinawakomera kuchita ichi, ndipo ndithu anali ndi ngongole kwa iwo. Pakuti ngati a mitundu ina anagawana ndi Ayuda madalitso auzimu, iwo ali ndi ngongole kwa Ayuda kuti agawane nawo madalitso awo a ku thupi.
28 Bu işi bitirip sağlanan yardımı onlara ulaştırdıktan sonra size uğrayacağım, sonra da İspanya'ya gideceğim.
Tsono ine nditamaliza ntchito iyi ndi kutsimikiza kuti alandira chipatsochi, ndidzadzera kwanuko kudzakuchezerani pa ulendo wanga popita ku Spaniya.
29 Yanınıza geldiğimde, Mesih'in bereketinin doluluğuyla geleceğimi biliyorum.
Ine ndikudziwa kuti pamene ndidzabwera kwa inu, ndidzafika ndili wodzaza ndi madalitso a Khristu.
30 Kardeşler, Rabbimiz İsa Mesih ve Ruh'un sevgisi adına size yalvarıyorum, benim için Tanrı'ya dua ederek uğraşıma katılın.
Abale, ine ndikukupemphani, mwa Ambuye athu Yesu Khristu ndi mwachikondi cha Mzimu, kuti mukhale nane pa kulimbika kwanga pondipempherera kwa Mulungu.
31 Yahudiye'deki imansızlardan kurtulmam için ve Yeruşalim'e olan hizmetimin kutsallarca kabul edilmesi için dua edin.
Pempherani kuti ine ndilanditsidwe kwa osakhulupirira a ku Yudeya ndi kuti utumiki wanga mu Yerusalemu ukhale ovomerezeka ndi oyera mtima.
32 Öyle ki, Tanrı'nın isteğiyle sevinçle yanınıza gelip sizlerle gönlümü ferahlatayım.
Kuti mwachifuniro cha Mulungu ndibwere kwa inu ndi chimwemwe kuti ndidzapumule pamodzi ndi inu.
33 Esenlik veren Tanrı hepinizle birlikte olsun! Amin.
Mulungu wamtendere akhale ndi inu nonse. Ameni.

< Romalilar 15 >