< Vahiy 14 >

1 Sonra Kuzu'nun Siyon Dağı'nda durduğunu gördüm. O'nunla birlikte 144 000 kişi vardı. Alınlarında kendisinin ve Babası'nın adları yazılıydı.
Kenaka ndinaona patsogolo panga panali Mwana Wankhosa, atayimirira pa Phiri la Ziyoni, ndipo Iye anali pamodzi ndi anthu 144,000 amene pa mphumi pawo panalembedwa dzina la Mwana Wankhosayo ndi la Atate ake.
2 Gökten, gürül gürül akan suların sesini, güçlü gök gürlemesini andıran bir ses işittim. İşittiğim ses, lir çalanların çıkardığı sese benziyordu.
Ndipo ndinamva liwu lochokera kumwamba ngati mkokomo wa madzi ambiri, ndiponso ngati kugunda kwamphamvu kwa bingu. Liwu limene ndinamvalo linali ngati a anthu akuyimba azeze awo.
3 Bu 144 000 kişi, tahtın önünde, dört yaratığın ve ihtiyarların önünde yeni bir ezgi söylüyordu. Yeryüzünden satın alınmış olan bu kişilerden başka kimse o ezgiyi öğrenemedi.
Anthuwo ankayimba nyimbo yatsopano patsogolo pa mpando waufumu ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kuphunzira nyimboyo kupatula anthu 144,000 aja amene anawomboledwa pa dziko lapansi.
4 Kendilerini kadınlarla lekelememiş olanlar bunlardır. Pak kişilerdir. Kuzu nereye giderse ardısıra giderler. Tanrı'ya ve Kuzu'ya ait olacakların ilk bölümü olmak üzere insanlar arasından satın alınmışlardır.
Awa ndiwo amene sanadzidetse koma anadzisunga ndipo sanadziyipitse ndi akazi. Anthu amenewa ndiwo ankatsatira Mwana Wankhosa kulikonse kumene ankapita. Ndiwo amene anagulidwa pakati pa anthu a dziko lapansi kuti akhale oyambirira kuperekedwa kwa Mulungu ndi kwa Mwana Wankhosa.
5 Ağızlarından hiç yalan çıkmamıştır. Kusursuzdurlar.
Iwo sananenepo bodza ndipo alibe cholakwa.
6 Bundan sonra göğün ortasında uçan başka bir melek gördüm. Yeryüzünde yaşayanlara –her ulusa, her oymağa, her dile, her halka– iletmek üzere sonsuza dek kalıcı olan Müjde'yi getiriyordu. (aiōnios g166)
Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. (aiōnios g166)
7 Yüksek sesle şöyle diyordu: “Tanrı'dan korkun! O'nu yüceltin! Çünkü O'nun yargılama saati geldi. Göğü, yeri, denizi, su pınarlarını yaratana tapının!”
Mngeloyo anayankhula mokweza mawu kuti, “Wopani Mulungu ndi kumutamanda, chifukwa nthawi yoweruza anthu yafika. Mumupembedze Iye amene analenga thambo, dziko lapansi, nyanja ndi akasupe amadzi.”
8 Ardından gelen ikinci bir melek, “Yıkıldı! Kendi azgın fuhuş şarabını bütün uluslara içiren büyük Babil yıkıldı!” diyordu.
Mngelo wachiwiri anatsatana naye ndipo anati, “Wagwa! Wagwa Babuloni womveka uja, amene anachititsa anthu a mitundu yonse kumwa vinyo wa zilakolako zake zachigololo.”
9 Onları üçüncü bir melek izledi. Yüksek sesle şöyle diyordu: “Bir kimse canavara ve heykeline taparsa, alnına ya da eline canavarın işaretini koydurursa, Tanrı gazabının kâsesinde saf olarak hazırlanmış Tanrı öfkesinin şarabından içecektir. Böylelerine kutsal meleklerin ve Kuzu'nun önünde ateş ve kükürtle işkence edilecek.
Mngelo wachitatu anatsatana nawo ndi mawu ofuwula anati, “Ngati wina apembedza chirombo chija ndi fano lake ndi kulembedwa chizindikiro pa mphumi kapena pa dzanja,
nayenso adzamwa vinyo waukali wa Mulungu, umene wathiridwa popanda kuchepetsa mphamvu zake mʼchikho cha ukali wa Mulungu. Munthuyo adzazunzidwa ndi moto wamiyala yasulufure pamaso pa angelo oyera ndi pa Mwana Wankhosa.
11 Çektikleri işkencenin dumanı sonsuzlara dek tütecek. Canavara ve heykeline tapıp onun adının işaretini alanlar gece gündüz rahat yüzü görmeyecekler. (aiōn g165)
Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” (aiōn g165)
12 Bu da, Tanrı'nın buyruklarını yerine getiren, İsa'ya imanlarını sürdüren kutsalların sabrını gerektirir.”
Pamenepa ndi pofunika kupirira kwa anthu oyera mtima amene amasunga malamulo a Mulungu ndi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu.
13 Gökten bir ses işittim. “Yaz! Bundan böyle Rab'be ait olarak ölenlere ne mutlu!” diyordu. Ruh, “Evet” diyor, “Uğraşlarından dinlenecekler. Çünkü yaptıkları onları izleyecek.”
Kenaka ndinamva mawu kuchokera kumwamba akuti, “Lemba kuti, Odala anthu amene akufa ali mwa Ambuye kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo.” “Inde,” akutero Mzimu, “akapumule ntchito zawo zotopetsa pakuti ntchito zawo zidzawatsata.”
14 Sonra beyaz bir bulut gördüm. Bulutun üzerinde “insanoğluna benzer biri” oturuyordu. Başında altın bir taç, elinde keskin bir orak vardı.
Ndinayangʼana patsogolo panga ndinaona mtambo woyera patakhalapo wina ngati Mwana wa Munthu, kumutu atavala chipewa chaufumu chagolide ndipo mʼdzanja mwake munali chikwakwa chakunthwa.
15 Tapınaktan çıkan başka bir melek bulutun üzerinde oturana yüksek sesle bağırdı: “Orağını uzat ve biç! Biçme saati geldi. Çünkü yerin ekini olgunlaşmış bulunuyor.”
Tsono mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu nafuwula mwamphamvu kwa uja wokhala pa mtamboyu. Mngeloyo anati, “Tenga chikwakwa chako ndipo kolola, pakuti nthawi yokolola ya dziko la pansi yakwana”
16 Bulutun üzerinde oturan, orağını yerin üzerine salladı, yerin ekini biçildi.
Choncho wokhala pa mtambo uja anayamba kukolola dzinthu pa dziko lapansi ndi chikwakwa chakecho.
17 Gökteki tapınaktan başka bir melek çıktı. Onun da keskin bir orağı vardı.
Mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu kumwamba ndipo nayenso anali ndi chikwakwa chakunthwa.
18 Ateş üzerinde yetkili olan başka bir melek de sunaktan çıkıp geldi. Keskin orağı olana yüksek sesle, “Keskin orağını uzat!” dedi. “Yerin asmasının salkımlarını topla. Çünkü üzümleri olgunlaştı.”
Kenaka mngelo winanso amene amalamulira moto, anatuluka kuchokera ku guwa lansembe nayitana mwamphamvu mngelo uja amene anali ndi chikwakwa chakunthwa chija, nati, “Tenga chikwakwa chako chakunthwacho yamba kudula mphesa za mʼmunda wamphesa wa pa dziko lapansi, pakuti mphesa zapsa kale.”
19 Bunun üzerine melek orağını yerin üzerine salladı. Yerin asmasının ürününü toplayıp Tanrı öfkesinin büyük masarasına attı.
Pamenepo mngeloyo anayambadi kugwiritsa ntchito chikwakwa chake nadula mphesa za dziko lapansi, naziponya mʼchopondera mphesa chachikulu cha ukali woopsa wa Mulungu.
20 Kentin dışında çiğnenen masaradan kan aktı. Kan, 1 600 ok atımı kadar yayılıp atların gemlerine dek yükseldi.
Mphesazo zinapondedwa mʼchopondera mphesa kunja kwa mzinda. Mʼchopondera mphesamo munatuluka magazi amene anayenderera ngati mtsinje, kuzama kwake mita ndi theka ndipo kutalika kwake makilomita 300.

< Vahiy 14 >