< Mezmurlar 9 >

1 Müzik şefi için - “Oğulun Ölümü” makamında - Davut'un mezmuru Ya RAB, bütün yüreğimle sana şükredeceğim, Yaptığın harikaların hepsini anlatacağım.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Sende sevinç bulacak, coşacağım, Adını ilahilerle öveceğim, ey Yüceler Yücesi!
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Düşmanlarım geri çekilirken, Sendeleyip ölüyorlar senin önünde.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Çünkü hakkımı, davamı sen savundun, Adil yargıç olarak tahta oturdun.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Ulusları azarladın, kötüleri yok ettin, Sonsuza dek adlarını sildin.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Yok olup gitti düşmanlar sonsuza dek, Kökünden söktün kentlerini, Anıları bile silinip gitti.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Oysa RAB sonsuza dek egemenlik sürer, Yargı için kurmuştur tahtını;
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 O yönetir doğrulukla dünyayı, O yargılar adaletle halkları.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 RAB ezilenler için bir sığınak, Sıkıntılı günlerde bir kaledir.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 Seni tanıyanlar sana güvenir, Çünkü sana yönelenleri hiç terk etmedin, ya RAB.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Siyon'da oturan RAB'bi ilahilerle övün! Yaptıklarını halklar arasında duyurun!
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Çünkü dökülen kanın hesabını soran anımsar, Ezilenlerin feryadını unutmaz.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Acı bana, ya RAB! Ey beni ölümün eşiğinden kurtaran, Benden nefret edenler yüzünden çektiğim sıkıntıya bak!
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 Öyle ki, övgüye değer işlerini anlatayım, Siyon Kenti'nin kapılarında Sağladığın kurtuluşla sevineyim.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Uluslar kendi kazdıkları kuyuya düştü, Ayakları gizledikleri ağa takıldı.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Adil yargılarıyla RAB kendini gösterdi, Kötüler kendi kurdukları tuzağa düştü. Higayon (sela)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 Kötüler ölüler diyarına gidecek, Tanrı'yı unutan bütün uluslar... (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 Ama yoksul büsbütün unutulmayacak, Mazlumun umudu sonsuza dek kırılmayacak.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Kalk, ya RAB! İnsan galip çıkmasın, Huzurunda yargılansın uluslar!
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Onlara dehşet saç, ya RAB! Sadece insan olduklarını bilsin uluslar. (Sela)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Mezmurlar 9 >