< Mezmurlar 66 >

1 Müzik şefi için - İlahi - Mezmur Ey yeryüzündeki bütün insanlar, Tanrı'ya sevinç çığlıkları atın!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Adının yüceliğine ilahiler söyleyin, O'na görkemli övgüler sunun!
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 “Ne müthiş işlerin var!” deyin Tanrı'ya, “Öyle büyük gücün var ki, Düşmanların eğiliyor önünde.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Bütün yeryüzü sana tapınıyor, İlahiler okuyor, adını ilahilerle övüyor.” (Sela)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Gelin, bakın Tanrı'nın neler yaptığına! Ne müthiş işler yaptı insanlar arasında:
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 Denizi karaya çevirdi, Atalarımız yaya geçtiler ırmaktan. Yaptığına sevindik orada.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 Kudretiyle sonsuza dek egemenlik sürer, Gözleri ulusları süzer; Başkaldıranlar gurura kapılmasın! (Sela)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Ey halklar, Tanrımız'a şükredin, Övgülerini duyurun.
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 Hayatımızı koruyan, Ayaklarımızın kaymasına izin vermeyen O'dur.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 Sen bizi sınadın, ey Tanrı, Gümüş arıtır gibi arıttın.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 Ağa düşürdün bizi, Sırtımıza ağır yük vurdun.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 İnsanları başımıza çıkardın, Ateşten, sudan geçtik. Ama sonra bizi bolluğa kavuşturdun.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 Yakmalık sunularla evine gireceğim, Adaklarımı yerine getireceğim,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Sıkıntı içindeyken dudaklarımdan dökülen, Ağzımdan çıkan adakları.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Yakılan koçların dumanıyla semiz hayvanlardan Sana yakmalık sunular sunacağım, Tekeler, sığırlar kurban edeceğim. (Sela)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Gelin, dinleyin, ey sizler, Tanrı'dan korkanlar, Benim için neler yaptığını size anlatayım.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 Ağzımla O'na yakardım, Övgüsü dilimden düşmedi.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Yüreğimde kötülüğe yer verseydim, Rab beni dinlemezdi.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 Oysa Tanrı dinledi beni, Kulak verdi duamın sesine.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Övgüler olsun Tanrı'ya, Çünkü duamı geri çevirmedi, Sevgisini benden esirgemedi.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Mezmurlar 66 >