< Çölde Sayim 23 >

1 Balam Balak'a, “Burada benim için yedi sunak kur ve yedi boğayla yedi koç hazırla” dedi.
Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
2 Balak onun dediğini yaptı. Balak'la Balam her sunağın üstünde birer boğayla koç sundular.
Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
3 Sonra Balam Balak'a, “Ben az öteye gideceğim, sen yakmalık sununun yanında bekle” dedi, “Olur ki, RAB karşıma çıkar. Bana ne açıklarsa, sana bildiririm.” Sonra çıplak bir tepeye çıktı.
Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
4 Tanrı Balam'a göründü. Balam Tanrı'ya, “Yedi sunak kurdum, her sunağın üstünde birer boğayla koç sundum” dedi.
Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
5 RAB Balam'a ne söylemesi gerektiğini bildirerek, “Balak'a git, ona şu haberi ilet” dedi.
Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
6 Böylece Balam Balak'ın yanına döndü. Onun Moav önderleriyle birlikte yakmalık sunusunun yanında durduğunu gördü.
Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
7 Sonra şu bildiriyi iletti: “Balak beni Aram'dan, Moav Kralı beni doğu dağlarından getirdi. ‘Gel, benim için Yakup soyuna lanet oku’ dedi, ‘Gel, İsrail'in yıkımını dile.’
Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
8 Tanrı'nın lanetlemediğini Ben nasıl lanetlerim? RAB'bin yıkımını istemediği kişinin yıkımını Ben nasıl isteyebilirim?
Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
9 Kayaların doruğundan görüyorum onları, Tepelerden bakıyorum onlara. Tek başına yaşayan, Uluslardan kendini soyutlayan Bir halk görüyorum.
Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
10 Kim Yakup soyunun tozunu Ve İsrail'in dörtte birini sayabilir? Doğru kişilerin ölümüyle öleyim, Sonum onlarınki gibi olsun!”
Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
11 Balak Balam'a, “Bana ne yaptın?” dedi, “Düşmanlarıma lanet okuyasın diye seni getirdim. Oysa sen onları kutsadın!”
Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
12 Balam, “Ben ancak RAB'bin söylememi istediği şeyleri söylemeliyim” diye yanıtladı.
Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
13 Bunun üzerine Balak, “Ne olur, benimle gel” dedi, “Onları görebileceğin başka bir yere gidelim. Onların hepsini görmeyeceksin, bir kesimini göreceksin. Oradan onlara benim için lanet oku.”
Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
14 Böylece Balak Balam'ı Pisga Dağı'ndaki Gözcüler Yaylası'na götürdü. Orada yedi sunak kurdu, her sunağın üstünde birer boğayla koç sundu.
Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
15 Balam Balak'a, “Az ötede RAB'be danışacağım, sen burada yakmalık sununun yanında bekle” dedi.
Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
16 RAB Balam'a göründü, ne söylemesi gerektiğini bildirerek, “Balak'a git, ona şu haberi ilet” dedi.
Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
17 Böylece Balam Balak'ın yanına döndü, onun Moav önderleriyle birlikte yakmalık sunusunun yanında durduğunu gördü. Balak, “RAB ne dedi?” diye sordu.
Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
18 Balam şu bildiriyi iletti: “Ey Balak, uyan ve dinle; Ey Sippor oğlu, bana kulak ver.
Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
19 Tanrı insan değil ki, Yalan söylesin; İnsan soyundan değil ki, Düşüncesini değiştirsin. O söyler de yapmaz mı? Söz verir de yerine getirmez mi?
Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
20 Kutsamak için bana buyruk verildi; O kutsadı, ben değiştiremem.
Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
21 Yakup soyunda suç bulunmadı, Ne de İsrail'de kötülük. Tanrıları RAB aralarındadır, Aralarındaki kral olarak Adına sevinç çığlıkları atıyorlar.
“Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
22 Tanrı onları Mısır'dan çıkardı, O'nun yaban öküzü gibi gücü var.
Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
23 Yakup soyuna yapılan büyü tutmaz; İsrail'e karşı falcılık etkili olmaz. Şimdi Yakup ve İsrail için, ‘Tanrı neler yaptı!’ denecek.
Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
24 İşte halk bir dişi aslan gibi uyanıyor. Avını yiyip bitirmedikçe, Öldürülenlerin kanını içmedikçe rahat etmeyen aslan gibi kalkıyor.”
Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
25 Bunun üzerine Balak, “Onlara ne lanet oku, ne de onları kutsa!” dedi.
Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
26 Balam, “RAB ne derse onu yapmalıyım dememiş miydim sana?” diye yanıtladı.
“Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
27 Sonra Balak Balam'a, “Ne olur, gel, seni başka bir yere götüreyim” dedi, “Olur ki, Tanrı oradan benim için onlara lanet okumana izin verir.”
Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
28 Böylece Balam'ı çöle bakan Peor Dağı'nın tepesine götürdü.
Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
29 Balam, “Burada benim için yedi sunak kurup yedi boğayla yedi koç hazırla” dedi.
Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
30 Balak onun dediğini yaptı, her sunağın üstünde birer boğayla koç sundu.
Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.

< Çölde Sayim 23 >