< Luka 15 >

1 Bütün vergi görevlileriyle günahkârlar İsa'yı dinlemek için O'na akın ediyordu.
Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
2 Ferisiler'le din bilginleri ise, “Bu adam günahkârları kabul ediyor, onlarla birlikte yemek yiyor” diye söyleniyorlardı.
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
3 Bunun üzerine İsa onlara şu benzetmeyi anlattı: “Sizlerden birinin yüz koyunu olsa ve bunlardan bir tanesini kaybetse, doksan dokuzu bozkırda bırakarak kaybolanı bulana dek onun ardına düşmez mi?
Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
4
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
5 Onu bulunca da sevinç içinde omuzlarına alır, evine döner; arkadaşlarını, komşularını çağırıp onlara, ‘Benimle birlikte sevinin, kaybolan koyunumu buldum!’ der.
Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
6
ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
7 Size şunu söyleyeyim, aynı şekilde gökte, tövbe eden tek bir günahkâr için, tövbeyi gereksinmeyen doksan dokuz doğru kişi için duyulandan daha büyük sevinç duyulacaktır.”
Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
8 “Ya da on gümüş parası olan bir kadın bunlardan bir tanesini kaybetse, kandil yakıp evi süpürerek parayı bulana dek her tarafı dikkatle aramaz mı?
“Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
9 Parayı bulunca da arkadaşlarını, komşularını çağırıp, ‘Benimle birlikte sevinin, kaybettiğim parayı buldum!’ der.
Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
10 Size şunu söyleyeyim, aynı şekilde Tanrı'nın melekleri de tövbe eden bir tek günahkâr için sevinç duyacaklar.”
Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
11 İsa, “Bir adamın iki oğlu vardı” dedi.
Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
12 “Bunlardan küçüğü babasına, ‘Baba’ dedi, ‘Malından payıma düşeni ver bana.’ Baba da servetini iki oğlu arasında paylaştırdı.
Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
13 “Bundan birkaç gün sonra küçük oğul her şeyini toplayıp uzak bir ülkeye gitti. Orada sefahat içinde bir yaşam sürerek varını yoğunu çarçur etti.
“Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
14 Delikanlı her şeyini harcadıktan sonra, o ülkede şiddetli bir kıtlık baş gösterdi, o da yokluk çekmeye başladı.
Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
15 Bunun üzerine gidip o ülkenin vatandaşlarından birinin hizmetine girdi. Adam onu, domuz gütmek üzere otlaklarına yolladı.
Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
16 Delikanlı, domuzların yediği keçiboynuzlarıyla karnını doyurmaya can atıyordu. Ama hiç kimse ona bir şey vermedi.
Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
17 “Aklı başına gelince şöyle dedi: ‘Babamın nice işçisinin fazlasıyla yiyeceği var, bense burada açlıktan ölüyorum.
“Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
18 Kalkıp babamın yanına döneceğim, ona, Baba diyeceğim, Tanrı'ya ve sana karşı günah işledim.
Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
19 Ben artık senin oğlun olarak anılmaya layık değilim. Beni işçilerinden biri gibi kabul et.’
Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
20 “Böylece kalkıp babasının yanına döndü. Kendisi daha uzaktayken babası onu gördü, ona acıdı, koşup boynuna sarıldı ve onu öptü.
Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
21 Oğlu ona, ‘Baba’ dedi, ‘Tanrı'ya ve sana karşı günah işledim. Ben artık senin oğlun olarak anılmaya layık değilim.’
“Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
22 “Babası ise kölelerine, ‘Çabuk, en iyi kaftanı getirip ona giydirin!’ dedi. ‘Parmağına yüzük takın, ayaklarına çarık giydirin!
“Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
23 Besili danayı getirip kesin, yiyelim, eğlenelim.
Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
24 Çünkü benim bu oğlum ölmüştü, yaşama döndü; kaybolmuştu, bulundu.’ Böylece eğlenmeye başladılar.
Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
25 “Babanın büyük oğlu ise tarladaydı. Gelip eve yaklaştığında çalgı ve oyun seslerini duydu.
“Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
26 Uşaklardan birini yanına çağırıp, ‘Ne oluyor?’ diye sordu.
Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
27 “O da, ‘Kardeşin geldi, baban da ona sağ salim kavuştuğu için besili danayı kesti’ dedi.
Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
28 “Büyük oğul öfkelendi, içeri girmek istemedi. Babası dışarı çıkıp ona yalvardı. Ama o, babasına şöyle yanıt verdi: ‘Bak, bunca yıl senin için köle gibi çalıştım, hiçbir zaman buyruğundan çıkmadım. Ne var ki sen bana, arkadaşlarımla eğlenmem için hiçbir zaman bir oğlak bile vermedin.
“Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
30 Oysa senin malını fahişelerle yiyen şu oğlun eve dönünce, onun için besili danayı kestin.’
Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
31 “Babası ona, ‘Oğlum, sen her zaman yanımdasın, neyim varsa senindir’ dedi.
Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
32 ‘Ama sevinip eğlenmek gerekiyordu. Çünkü bu kardeşin ölmüştü, yaşama döndü; kaybolmuştu, bulundu!’”
Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”

< Luka 15 >