< Eyüp 8 >

1 Şuahlı Bildat şöyle yanıtladı:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Ne zamana dek böyle konuşacaksın? Sözlerin sert rüzgar gibi.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Tanrı adaleti saptırır mı, Her Şeye Gücü Yeten doğru olanı çarpıtır mı?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Oğulların ona karşı günah işlediyse, İsyanlarının cezasını vermiştir.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Ama sen gayretle Tanrı'yı arar, Her Şeye Gücü Yeten'e yalvarırsan,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Temiz ve doğruysan, O şimdi bile senin için kolları sıvayıp Seni hak ettiğin yere geri getirecektir.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Başlangıcın küçük olsa da, Sonun büyük olacak.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 “Lütfen, önceki kuşaklara sor, Atalarının neler öğrendiğini iyice araştır.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Çünkü biz daha dün doğduk, bir şey bilmeyiz, Yeryüzündeki günlerimiz sadece bir gölge.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Onlar sana anlatıp öğretmeyecek, İçlerindeki sözleri dile getirmeyecek mi?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 “Bataklık olmayan yerde kamış biter mi? Susuz yerde saz büyür mü?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Henüz yeşilken, kesilmeden, Otlardan önce kururlar.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tanrı'yı unutan herkesin sonu böyledir, Tanrısız insanın umudu böyle yok olur.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Onun güvendiği şey kırılır, Dayanağı ise bir örümcek ağıdır.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Örümcek ağına yaslanır, ama ağ çöker, Ona tutunur, ama ağ taşımaz.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Tanrısızlar güneşte iyi sulanmış bitkiyi andırır, Dalları bahçenin üzerinden aşar;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Kökleri taş yığınına sarılır, Çakılların arasında yer aranır.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Ama yerinden sökülürse, Yeri, ‘Seni hiç görmedim’ diyerek onu yadsır.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 İşte sevinci böyle son bulur, Yerinde başka bitkiler biter.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 “Tanrı kusursuz insanı reddetmez, Kötülük edenlerin elinden tutmaz.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 O senin ağzını yine gülüşle, Dudaklarını sevinç haykırışıyla dolduracaktır.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Düşmanlarını utanç kaplayacak, Kötülerin çadırı yok olacaktır.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Eyüp 8 >