< Eyüp 15 >

1 Temanlı Elifaz şöyle yanıtladı:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 “Bilge kişi boş sözlerle yanıtlar mı, Karnını doğu rüzgarıyla doldurur mu?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Boş sözlerle tartışır, Yararsız söylevler verir mi?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Tanrı korkusunu bile ortadan kaldırıyor, Tanrı'nın huzurunda düşünmeyi engelliyorsun.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Çünkü suçun ağzını kışkırtıyor, Hilekârların diliyle konuşuyorsun.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Kendi ağzın seni suçluyor, ben değil, Dudakların sana karşı tanıklık ediyor.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 “İlk doğan insan sen misin? Yoksa dağlardan önce mi var oldun?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Tanrı'nın sırrını mı dinledin de, Yalnız kendini bilge görüyorsun?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Senin bildiğin ne ki, biz bilmeyelim? Senin anladığın ne ki, bizde olmasın?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Bizde ak saçlı da yaşlı da var, Babandan bile yaşlı.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Az mı geliyor Tanrı'nın avutması sana, Söylediği yumuşak sözler?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Niçin yüreğin seni sürüklüyor, Gözlerin parıldıyor,
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Tanrı'ya öfkeni gösteriyorsun, Ağzından böyle sözler dökülüyor?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 “İnsan gerçekten temiz olabilir mi? Kadından doğan biri doğru olabilir mi?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Tanrı meleklerine güvenmiyorsa, Gökler bile O'nun gözünde temiz değilse,
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Haksızlığı su gibi içen İğrenç, bozuk insana mı güvenecek?
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 “Dinle beni, sana açıklayayım, Gördüğümü anlatayım,
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Bilgelerin atalarından öğrenip bildirdiği, Gizlemediği gerçekleri;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 O atalar ki, ülke yalnız onlara verilmişti, Aralarına henüz yabancı girmemişti.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Kötü insan yaşamı boyunca kıvranır, Zorbaya ayrılan yıllar sayılıdır.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Dehşet sesleri kulağından eksilmez, Esenlik içindeyken soyguncunun saldırısına uğrar.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Karanlıktan kurtulabileceğine inanmaz, Kılıç onu gözler.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 ‘Nerede?’ diyerek ekmek ardınca dolaşır, Karanlık günün yanıbaşında olduğunu bilir.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Acı ve sıkıntı onu yıldırır, Savaşa hazır bir kral gibi onu yener.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Çünkü Tanrı'ya el kaldırmış, Her Şeye Gücü Yeten'e meydan okumuş,
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Kalın, yumrulu kalkanıyla O'na inatla saldırmıştı.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 “Yüzü semirdiği, Göbeği yağ bağladığı halde,
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 Yıkılmış kentlerde, Taş yığınına dönmüş oturulmaz evlerde oturacak,
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Zengin olmayacak, serveti tükenecek, Malları ülkeye yayılmayacaktır.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Karanlıktan kaçamayacak, Filizlerini alev kurutacak, Tanrı'nın ağzından çıkan solukla yok olacaktır.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Boş şeye güvenerek kendini aldatmasın, Çünkü ödülü de boş olacaktır.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Gününden önce işi tamamlanacak, Dalı yeşermeyecektir.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Asma gibi koruğunu dökecek, Zeytin ağacı gibi çiçeğini dağıtacaktır.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Çünkü tanrısızlar sürüsü kısır olur, Rüşvetçilerin çadırlarını ateş yakıp yok eder.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Fesada gebe kalıp kötülük doğururlar, İçleri yalan doludur.”
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Eyüp 15 >