< Yeremya 49 >

1 RAB Ammonlular'a ilişkin şöyle diyor: “İsrail'in çocukları yok mu? Yok mu mirasçısı? Öyleyse neden ilah Molek Gad'ı mülk edindi? Neden onun halkı Gad kentlerinde oturuyor?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 İşte bu nedenle” diyor RAB, “Ammonlular'ın Rabba Kenti'ne karşı Savaş narasını işittireceğim günler geliyor. Rabba ıssız bir höyük olacak, Köyleri ateşe verilecek. Böylece İsrail, kendisini mülk edinenleri Mülk edinecek” diyor RAB.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 “Haykır, ey Heşbon! Ay Kenti yıkıldı! Feryat edin, ey Rabba kızları! Çul sarınıp yas tutun. Duvarların arasında oraya buraya koşuşun. Çünkü Molek kâhinleri ve görevlileriyle birlikte Sürgüne gönderilecek.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Verimli vadilerinle ne kadar övünüyorsun, Ey dönek kız! Servetine güvenerek, ‘Bana kim saldırabilir?’ diyorsun.
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Bütün çevrenden Dehşet saçacağım üzerine” Diyor Rab, Her Şeye Egemen RAB. “Her biriniz apar topar sürülecek, Kaçkınları toplayan olmayacak.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 Ama sonra Ammonlular'ı Eski gönencine kavuşturacağım” diyor RAB.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Her Şeye Egemen RAB Edom'a ilişkin şöyle diyor: “Teman Kenti'nde bilgelik kalmadı mı artık? Akıllı kişilerde öğüt tükendi mi? Bilgelikleri yozlaştı mı?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Kaçın, geri dönün, derinliklere sığının, Ey Dedan'da yaşayanlar! Çünkü Esav'ı cezalandırdığımda Başına felaket getireceğim.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Üzüm toplayanlar bağına girseydi, Birkaç salkım bırakmazlar mıydı? Gece hırsızlar gelselerdi, Yalnızca gereksindiklerini çalmazlar mıydı?
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Oysa ben Esav'ı çırılçıplak soyacak, Gizli yerlerini açığa çıkaracağım, Gizlenemeyecek. Çocukları, akrabaları, komşuları Yıkıma uğrayacak. Kendisi de yok olacak!
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Öksüz çocuklarını bırak, Ben yaşatırım onları. Dul kadınların da bana güvensinler.”
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 RAB diyor ki, “Hak etmeyenler bile kâseyi içmek zorundayken, Sen mi cezasız kalacaksın? Hayır, cezasız kalmayacaksın, Kesinlikle içeceksin kâseyi.
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Adım üzerine ant içerim ki” diyor RAB, “Bosra dehşet konusu olacak, yerilecek, Viraneye dönecek, aşağılanacak. Bütün kentleri sonsuza dek yıkık kalacak.”
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 RAB'den bir haber aldım: Uluslara gönderdiği haberci, “Edom'a saldırmak için toplanın, Savaşa hazırlanın!” diyor.
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 “Bak, seni uluslar arasında küçük düşüreceğim, İnsanlar seni hor görecek.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Saçtığın dehşet ve yüreğindeki gurur Seni aldattı. Sen ki, kaya kovuklarında yaşıyor, Tepenin doruğunu elinde tutuyorsun. Yuvanı kartal gibi yükseklerde kursan da, Oradan indireceğim seni” diyor RAB.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 “Edom dehşet konusu olacak, Oradan geçen herkes şaşkın şaşkın bakıp Başına gelen belalardan ötürü Onunla alay edecek.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Sodom'la Gomora'yı ve çevredeki köyleri Nasıl yerle bir ettimse” diyor RAB, “Orada da kimse oturmayacak, İnsan oraya yerleşmeyecek.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 “Şeria çalılıklarından Sulak otlağa çıkan aslan gibi Edom'u bir anda yurdundan kovacağım. Seçeceğim kişiyi ona yönetici atayacağım. Var mı benim gibisi? Var mı bana dava açacak biri, Bana karşı duracak çoban?”
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Bu yüzden RAB'bin Edom'a karşı ne tasarladığını, Teman'da yaşayanlara karşı ne amaçladığını işitin: “Sürünün küçükleri bile sürülecek, Halkı yüzünden Edom otlakları çöle dönüştürülecek.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Yıkılışlarının gürültüsünden yeryüzü titreyecek, Çığlıkları Kamış Denizi'ne dek duyulacak.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Düşman kartal gibi üzerlerine çullanacak, Kanatlarını Bosra'ya karşı açacak. O gün Edomlu askerlerin yüreği, Doğum sancısı çeken kadının yüreği gibi olacak.”
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Şam'a ilişkin: “Hama ve Arpat utanacak, Çünkü kötü haber işittiler. Korkudan eridiler, Sessiz duramayan deniz gibi Kaygıyla sarsıldılar.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 “Şam güçsüz düştü, Kaçmak için döndü; Telaşa kapıldı, Doğuran kadın gibi Sancı ve acılar sardı onu.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Nasıl oldu da sevinç bulduğum ünlü kent Terk edilmedi?
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Bu yüzden gençleri meydanlarda düşecek, Bütün savaşçıları susturulacak o gün” Diyor Her Şeye Egemen RAB.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Şam surlarını ateşe vereceğim, Yakıp yok edecek Ben-Hadat'ın saraylarını.”
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Babil Kralı Nebukadnessar'ın bozguna uğrattığı Kedar ve Hasor krallıklarına ilişkin RAB şöyle diyor: “Kalkın, Kedar'a saldırın, Doğu halkını yok edin.
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Çadırlarıyla sürüleri alınacak, Çadır perdeleri, Eşyalarıyla develeri alınıp götürülecek. İnsanlar, ‘Her yer dehşet içinde!’ diye bağıracaklar onlara.
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Kaçın, uzaklaşın! Derinliklere sığının, Ey Hasor'da oturanlar!” diyor RAB. “Çünkü Babil Kralı Nebukadnessar Size düzen kurdu; Sizin için bir tasarısı var.
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 Kalkın, tasasız ve güvenlik içinde Yaşayan ulusa saldırın” diyor RAB. “Onun kent kapıları, sürgüleri yok, Halkı tek başına yaşıyor.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Develeri yağma edilecek, Sayısız sürüleri çapul malı olacak. Zülüflerini kesenleri Dört yana dağıtacağım, Her yandan felaket getireceğim başlarına” diyor RAB.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 “Çakalların uğrağı Hasor, Sonsuza dek viran kalacak, Orada kimse oturmayacak, İnsan oraya yerleşmeyecek.”
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Yahuda Kralı Sidkiya'nın krallığının başlangıcında RAB'bin Peygamber Yeremya'ya bildirdiği Elam'a ilişkin söz şudur:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “Bakın, Elam'ın yayını, Asıl gücünü kıracağım.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Üzerine göğün dört ucundan Dört rüzgarı gönderecek, Halkını bu rüzgarlara dağıtacağım. Elam sürgünlerinin gitmediği Bir ulus kalmayacak.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 Düşmanlarının önünde, Can düşmanlarının önünde Elam'ı darmadağın edeceğim. Başlarına felaket gönderecek, Şiddetli öfkemi yağdıracağım” diyor RAB, “Onları büsbütün yok edene dek Peşlerine kılıcı salacağım.
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Elam'da tahtımı kuracak, Elam Kralı'yla önderlerini Yok edeceğim” diyor RAB.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 “Ama son günlerde Elam'ı eski gönencine kavuşturacağım” diyor RAB.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Yeremya 49 >