< Yeremya 15 >

1 RAB bana dedi ki, “Musa'yla Samuel önümde durup yalvarsalar bile, bu halka acımayacağım; kov onları önümden, gitsinler!
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Sana, ‘Nereye gidelim?’ diye sorarlarsa de ki, ‘RAB şöyle diyor: “‘Ölüm için ayrılanlar ölüme, Kılıç için ayrılanlar kılıca, Kıtlık için ayrılanlar kıtlığa, Sürgün için ayrılanlar sürgüne.’
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 “Onların başına dört tür yıkım getirmeye karar verdim” diyor RAB, “Öldürmek için kılıcı, paralamak için köpekleri, yiyip bitirmek, yok etmek için yırtıcı kuşlarla yabanıl hayvanları salacağım üzerlerine.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Yahuda Kralı Hizkiya oğlu Manaşşe'nin Yeruşalim'de yaptıkları yüzünden bütün yeryüzü krallıklarını dehşete düşüreceğim.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 “Kim acıyacak sana, ey Yeruşalim? Kim yas tutacak senin için? Hal hatır sormak için Kim yolundan dönüp sana gelecek?
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Sen beni reddettin” diyor RAB, “Gerisingeri gidiyorsun. Ben de elimi sana karşı kaldıracak, Seni yok edeceğim; Merhamet ede ede yoruldum.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Ülkenin kapılarında, Halkımı yabayla savuracak, Çocuksuz bırakacak, yok edeceğim; Çünkü yollarından dönmediler.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Dul kadınlarının sayısı denizin kumundan çok olacak. Gençlerinin annelerine Öğle vakti yok ediciyi göndereceğim; Üzerlerine ansızın acı, dehşet salacağım.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Yedi çocuklu kadın Bayılıp son soluğunu verecek; Daha gündüzken güneşi batacak, Utandırılıp alçaltılacak. Sağ kalanları düşmanlarının önünde Kılıca teslim edeceğim.” Böyle diyor RAB.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Vay başıma! Herkesle çekişip davacı olayım diye Doğurmuşsun beni, ey annem! Ne ödünç aldım, ne de verdim, Yine de herkes lanet okuyor bana.
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 RAB şöyle dedi: “Kuşkun olmasın, iyilik için seni özgür kılacağım, Yıkım ve sıkıntı zamanında Düşmanlarını sana yalvartacağım.
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 “Demiri, kuzeyden gelen demiri Ya da tuncu kimse kırabilir mi?
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Ülkende işlenen günahlar yüzünden Servetini de hazinelerini de karşılıksız, Çapul malı olarak vereceğim.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 Bilmediğin bir ülkede Düşmanlarına köle edeceğim seni. Çünkü size karşı öfkem Ateş gibi tutuşup yanacak.”
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 Sen bilirsin, ya RAB, Beni anımsa, beni kolla. Bana eziyet edenlerden öcümü al. Sabrınla beni canımdan etme, Senin uğruna aşağılandığımı unutma.
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Sözlerini bulur bulmaz yuttum, Bana neşe, yüreğime sevinç oldu. Çünkü seninim ben, Ya RAB, Her Şeye Egemen Tanrı!
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Eğlenenlerin arasında oturmadım, Onlarla sevinip coşmadım. Elin üzerimde olduğu için Tek başıma oturdum, Çünkü beni öfkeyle doldurmuştun.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Neden sürekli acı çekiyorum? Neden yaram ağır ve umarsız? Benim için aldatıcı bir dere, Güvenilmez bir pınar mı olacaksın?
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Bu yüzden RAB diyor ki, “Eğer dönersen seni yine hizmetime alırım; İşe yaramaz sözler değil, Değerli sözler söylersen, Benim sözcüm olursun. Bu halk sana dönecek, Ama sen onlara dönmemelisin.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Bu halkın karşısında Sağlamlaştırılmış tunç bir duvar kılacağım seni; Seninle savaşacak ama yenemeyecekler, Çünkü yardım etmek, kurtarmak için Ben seninleyim” diyor RAB.
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 “Seni kötünün elinden kurtaracak, Acımasızın avucundan kurtaracağım.”
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Yeremya 15 >