< Yeşaya 9 >

1 Bununla birlikte sıkıntı çekmiş olan ülke karanlıkta kalmayacak. Geçmişte Zevulun ve Naftali bölgelerini alçaltan Tanrı, gelecekte Şeria Irmağı'nın ötesinde, Deniz Yolu'nda, ulusların yaşadığı Celile'yi onurlandıracak.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 Karanlıkta yürüyen halk Büyük bir ışık görecek; Ölümün gölgelediği diyarda Yaşayanların üzerine ışık parlayacak.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Ya RAB, ulusu çoğaltacak, sevincini artıracaksın. Ekin biçenlerin neşelendiği, Ganimet paylaşanların coştuğu gibi, Onlar da sevinecek senin önünde.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Çünkü onlara yük olan boyunduruğu, Omuzlarını döven değneği, Onlara eziyet edenlerin sopasını paramparça edeceksin; Tıpkı Midyanlılar'ı yenilgiye uğrattığın günkü gibi.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 Savaşta giyilen çizmeleri Ve kana bulanmış giysileri Yakılacak, ateşe yem olacak.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Çünkü bize bir çocuk doğacak, Bize bir oğul verilecek. Yönetim onun omuzlarında olacak. Onun adı Harika Öğütçü, Güçlü Tanrı, Ebedi Baba, Esenlik Önderi olacak.
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 Davut'un tahtı ve ülkesi üzerinde egemenlik sürecek. Egemenliğinin ve esenliğinin büyümesi son bulmayacak. Egemenliğini adaletle, doğrulukla kuracak Ve sonsuza dek sürdürecek. Her Şeye Egemen RAB'bin gayreti bunu sağlayacak.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 Rab İsrail için, Yakup soyu için yargısını bildirdi. Bu yargı yerine gelecek.
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 Bütün halk, Efrayim ve Samiriye'de yaşayanlar, Rab'bin bu yargısını duyacak. Gururlu ve küstah olan bu halk diyor ki,
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Kerpiç evler yıkıldı, Ama yerlerine yontma taştan evler yapacağız. Yabanıl incir ağaçları kesildi, Ama yerlerine sedir ağaçları dikeceğiz.”
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Bundan dolayı RAB, Resin'in hasımlarını Halka karşı güçlendirecek; Düşmanlarını, doğudan Aramlılar'ı, Batıdan Filistliler'i ayaklandıracak. Bunlar ağızlarını ardına kadar açıp İsrail'i yutacaklar. Bütün bunlara karşın RAB'bin öfkesi dinmedi, Eli hâlâ kalkmış durumda.
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 Halk kendisini cezalandıran RAB'be dönmeyecek, Her Şeye Egemen RAB'bi aramayacak.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Bunun için RAB İsrail'den başı da kuyruğu da Hurma dalını da sazı da Bir günde kesip atacak.
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 Baş ileri gelen saygın kişi, Kuyruksa öğretisi sahte olan peygamberdir.
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Çünkü bu halkı saptıranlar ona yol gösterenlerdir. Onları izleyenler de yem oluyor.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Bu yüzden Rab onların gençleri için sevinç duymayacak, Öksüzlerine, dul kadınlarına acımayacak. Çünkü hepsi tanrısızdır, kötülük yaparlar. Her ağız saçmalıyor. Bütün bunlara karşın RAB'bin öfkesi dinmedi, Eli hâlâ kalkmış durumda.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 Kötülük dikenli çalıları yiyip bitiren ateş gibidir. Ormandaki çalılığı tutuşturur, Duman sütunları yükseltir.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Her Şeye Egemen RAB'bin öfkesi Ülkeyi ateş gibi sardı. Halk ateşe yem olacak, Kardeş kardeşini esirgemeyecek.
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 İnsanlar şurada burada bulduklarını yiyecekler, Ama aç kalacak, doymayacaklar. Herkes çocuğunun etini yiyecek:
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manaşşe Efrayim'i, Efrayim Manaşşe'yi yiyecek, Sonra birlikte Yahuda'nın üzerine yürüyecekler. Bütün bunlara karşın RAB'bin öfkesi dinmedi, Eli hâlâ kalkmış durumda.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.

< Yeşaya 9 >