< Habakkuk 2 >

1 Nöbet yerinde, gözcü kulesinde durayım, Bakayım RAB bana ne diyecek, Yakınmalarıma ne yanıt verecek göreyim.
Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
2 Şöyle yanıtladı RAB: “Göreceklerini taş levhalara oyarak yaz. Öyle ki, herkes bir çırpıda okusun.
Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
3 Bu olayların zamanı gelmedi henüz. Sonun belirtileridir bunlar ve yalan değildir. Gecikiyormuş gibi görünse de bekle olacakları, Kesinlikle olacak, gecikmeyecek.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
4 Bakın şu övüngen kişiye, niyeti iyi değildir. Ama doğru kişi sadakatiyle yaşayacaktır.
“Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
5 Servet aldatıcıdır. Küstahlar kalıcı değildir; Açgözlüdürler ölüler diyarı gibi Ve ölüm gibi hiç doymazlar. Ülkeleri ele geçirip halkları tutsak alırlar. (Sheol h7585)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
6 Tutsak alınanlar onları küçümseyip alay etmeyecekler mi? ‘Kendisine ait olmayanı ele geçirenin, Haraç alarak zenginleşenin vay haline! Daha ne kadar sürecek bu?’ demeyecekler mi?
“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
7 Haraca kestikleriniz ansızın ayaklanmayacak mı? Uyanıp yakanıza yapışmayacaklar mı? İşte o zaman onlar için çapul malı gibi olacaksınız.
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
8 Birçok ulusu soyduğunuz, Kan döktüğünüz, Ülkelere, kentlere ve oralarda yaşayan herkese zorbalık ettiğiniz için, Halklardan sağ kalanlar da sizi soyacaklar.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
9 Evini haksız kazançla dolduranın, Felaketten kaçmak için yuvasını yüksek yere kuranın vay haline!
“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
10 Birçok halkı kıyıma uğratmakla Kendi soyunuzu utanca boğdunuz, Kendi yıkımınızı hazırladınız.
Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 Duvar taşları bile haykıracak bunu Ve yankılanacak ahşap kirişler.
Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
12 Kan dökerek kentler kuranın, Zorbalıkla beldeler yapanın vay haline!
“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Halkların bütün emeklerinin yanması, Ulusların bütün çabalarının boşa gitmesi Her Şeye Egemen RAB'bin işi değil mi?
Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 Çünkü sular denizi nasıl dolduruyorsa, Dünya da RAB'bin yüceliğinin bilgisiyle dolacak.
Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
15 Çıplak bedenlerini seyretmek için Komşularına içki içirip sarhoş eden, İçkiye zehir bile katan sizlerin vay haline!
“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
16 Onur yerine utanca boğulacaksınız. Şimdi sıra sizde, için de çıplaklığınız görünsün. RAB size sağ elindeki ceza dolu kâseden içirecek. Onurunuz kırılacak, rezil olacaksınız.
Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 Lübnan'a ettiğiniz zorbalık kendi başınıza gelecek. Telef ettiğiniz hayvanlar sizi dehşete düşürecek. Çünkü insan kanı döktünüz, Ülkelere, kentlere ve oralarda yaşayan herkese zorbalık ettiniz.
Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
18 İnsanın biçim verdiği oyma ya da dökme putun ne yararı var ki aldatmaktan başka? Putu yapan, yaptığına güvenir, Ama yaptığı ne ki, dilsiz puttan başka.
“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Tahta puta, ‘Canlan!’ diyenin, Dilsiz taşa, ‘Uyan’ diyenin Vay haline! Put yol gösterebilir mi? Altınla, gümüşle kaplanmış, Ama içinde yaşam soluğu yok.
Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 Oysa RAB kutsal tapınağındadır. Sussun bütün dünya O'nun önünde.”
Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

< Habakkuk 2 >