< Galatyalilar 5 >

1 Mesih bizi özgür olalım diye özgür kıldı. Bunun için dayanın. Bir daha kölelik boyunduruğuna girmeyin.
Khristu anatimasula kuti tikhale mfulu. Tsono chirimikani, ndipo musakodwenso mʼgoli la ukapolo.
2 Bakın, ben Pavlus size diyorum ki, sünnet olursanız Mesih'in size hiç yararı olmaz.
Chonde mvetsetsani! Ine Paulo, ndikukuwuzani kuti mukalola kuchita mdulidwe, Khristu simupindula nayenso konse.
3 Sünnet edilen her adamı bir daha uyarıyorum: Kutsal Yasa'nın tümünü yerine getirmek zorundadır.
Ndikubwerezanso kuwuza munthu aliyense wovomereza kuchita mdulidwe kuti ayeneranso kutsata Malamulo onse.
4 Yasa aracılığıyla aklanmaya çalışan sizler Mesih'ten ayrıldınız, Tanrı'nın lütfundan uzak düştünüz.
Inu amene mukufuna kulungamitsidwa ndi lamulo mwachotsedwa mwa Khristu; munagwa kusiyana nacho chisomo.
5 Ama biz aklanmanın verdiği umudun gerçekleşmesini Ruh'a dayanarak, imanla bekliyoruz.
Koma mwachikhulupiriro, ife tikudikira mwachidwi kudzera mwa Mzimu, chilungamo chimene tikuyembekeza.
6 Mesih İsa'da ne sünnetliliğin ne de sünnetsizliğin yararı vardır; yararlı olan, sevgiyle etkisini gösteren imandır.
Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe kapena kusachita mdulidwe zilibe phindu. Chinthu chokhacho chimene chimafunika ndi chikhulupiriro chogwira ntchito mwachikondi.
7 İyi koşuyordunuz. Sizi gerçeğe uymaktan kim alıkoydu?
Inu munkathamanga mpikisano wanu wabwino. Anakuletsani ndani kuti musamverenso choonadi?
8 Buna kanmanız sizi çağıranın isteği değildir.
Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Iye amene anakuyitanani.
9 “Azıcık maya bütün hamuru kabartır.”
“Yisiti wapangʼono amagwira ntchito mu buledi yense.”
10 Başka türlü düşünmeyeceğinize ilişkin Rab'de size güvenim var. Ama aklınızı karıştıran kim olursa olsun, cezasını çekecektir.
Ine ndikutsimikiza mwa Ambuye kuti inu simudzasiyana nane maganizo. Iye amene akukusokonezani adzalangidwa, kaya iyeyo ndiye ndani.
11 Bana gelince, kardeşler, eğer hâlâ sünneti savunuyor olsaydım, bugüne dek baskı görür müydüm? Öyle olsaydı, çarmıh engeli ortadan kalkardı.
Abale, ngati ine ndikulalikirabe za mdulidwe, nʼchifukwa chiyani ndikusautsidwabe? Ngati ndikanakhala kuti sindikulalikira chipulumutso cha mtanda, palibe amene akanakhumudwa.
12 Aklınızı çelenler keşke kendilerini hadım etseler!
Kunena za amene akukuvutani, ndikanakonda akanangodzithena okha!
13 Kardeşler, siz özgür olmaya çağrıldınız. Ancak özgürlük benlik için fırsat olmasın. Birbirinize sevgiyle hizmet edin.
Inu abale, Mulungu anakuyitanani kuti mukhale mfulu. Koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo kuchita zoyipa zachikhalidwe cha uchimo cha thupi lanu, koma mutumikirane wina ndi mnzake mwachikondi.
14 Bütün Kutsal Yasa tek bir sözde özetlenmiştir: “Komşunu kendin gibi seveceksin.”
Pakuti malamulo onse akuphatikizidwa mu lamulo ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.”
15 Ama birbirinizi ısırıp yiyorsanız, dikkat edin, birbirinizi yok etmeyesiniz!
Ngati mupitiriza kulumana ndi kukhadzulana, samalani kuti mungawonongane.
16 Şunu demek istiyorum: Kutsal Ruh'un yönetiminde yaşayın. O zaman benliğin tutkularını asla yerine getirmezsiniz.
Choncho ine ndikuti, mulole kuti Mzimu akutsogolereni ndipo simudzachita zofuna za thupi lanu la uchimo.
17 Çünkü benlik Ruh'a, Ruh da benliğe aykırı olanı arzular. Bunlar birbirine karşıttır; sonuç olarak, istediğinizi yapamıyorsunuz.
Pakuti thupi lanu la uchimo limalakalaka zimene ndi zotsutsana ndi Mzimu, ndi Mzimu zimene ndi zotsutsana ndi thupi lanu la uchimo. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mukufuna.
18 Ruh'un yönetimindeyseniz, Yasa'ya bağımlı değilsiniz.
Koma ngati Mzimu akutsogolerani, ndiye kuti simuli pansi pa lamulo.
19 Benliğin işleri bellidir. Bunlar fuhuş, pislik, sefahat, putperestlik, büyücülük, düşmanlık, çekişme, kıskançlık, öfke, bencil tutkular, ayrılıklar, bölünmeler, çekememezlik, sarhoşluk, çılgın eğlenceler ve benzeri şeylerdir. Sizi daha önce uyardığım gibi yine uyarıyorum, böyle davrananlar Tanrı Egemenliği'ni miras alamayacaklar.
Ntchito za thupi lanu la uchimo zimaonekera poyera ndi izi: dama, zodetsa ndi kuchita zonyansa;
kupembedza mafano ndi ufiti; kudana, kukangana, kupsa mtima, kudzikonda, kugawikana, mipatuko
ndi nsanje, kuledzera, mchezo ndi zina zotere. Ine ndikukuchenjezani monga ndinachita poyamba paja kuti amene amachita zimenezi sadzalandira ufumu wa Mulungu.
22 Ruh'un ürünüyse sevgi, sevinç, esenlik, sabır, şefkat, iyilik, bağlılık, yumuşak huyluluk ve özdenetimdir. Bu tür nitelikleri yasaklayan yasa yoktur.
Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika,
kufatsa ndi kudziretsa. Palibe lamulo loletsa zimenezi.
24 Mesih İsa'ya ait olanlar, benliği, tutku ve arzularıyla birlikte çarmıha germişlerdir.
Amene ali ake a Khristu Yesu anapachika pa mtanda thupi lawo la uchimo pamodzi ndi zokhumba zawo ndi zolakalaka zawo.
25 Ruh sayesinde yaşıyorsak, Ruh'un izinde yürüyelim.
Popeza timakhala ndi moyo mwa Mzimu Woyera, tiyeni tiyende pamodzi ndi Mzimu Woyera.
26 Boş yere övünen, birbirine meydan okuyan, birbirini kıskanan kişiler olmayalım.
Tisakhale odzitukumula, oputana ndi ochitirana nsanje.

< Galatyalilar 5 >