< Elçilerin İşleri 1 >

1 Ey Teofilos, İlk kitabımda İsa'nın yapıp öğretmeye başladığı her şeyi, seçmiş olduğu elçilere Kutsal Ruh aracılığıyla buyruklar verip yukarı alındığı güne dek olanları yazmıştım.
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 İsa, ölüm acısını çektikten sonra birçok inandırıcı kanıtlarla elçilere dirilmiş olduğunu gösterdi. Kırk gün süreyle onlara görünerek Tanrı'nın Egemenliği hakkında konuştu.
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 Kendileriyle birlikteyken onlara şu buyruğu vermişti: “Yeruşalim'den ayrılmayın, Baba'nın verdiği ve benden duyduğunuz sözün gerçekleşmesini bekleyin.
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 Şöyle ki, Yahya suyla vaftiz etti, ama sizler birkaç güne kadar Kutsal Ruh'la vaftiz edileceksiniz.”
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Elçiler bir araya geldiklerinde İsa'ya şunu sordular: “Ya Rab, İsrail'e egemenliği şimdi mi geri vereceksin?”
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 İsa onlara, “Baba'nın kendi yetkisiyle belirlemiş olduğu zamanları ve tarihleri bilmenize gerek yok” karşılığını verdi.
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 “Ama Kutsal Ruh üzerinize inince güç alacaksınız. Yeruşalim'de, bütün Yahudiye ve Samiriye'de ve dünyanın dört bucağında benim tanıklarım olacaksınız.”
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 İsa bunları söyledikten sonra, onların gözleri önünde yukarı alındı. Bir bulut O'nu alıp gözlerinin önünden uzaklaştırdı.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 İsa giderken onlar gözlerini göğe dikmiş bakıyorlardı. Tam o sırada, beyaz giysiler içinde iki adam yanlarında belirdi.
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 “Ey Celileliler, neden göğe bakıp duruyorsunuz?” diye sordular. “Aranızdan göğe alınan İsa, göğe çıktığını nasıl gördünüzse, aynı şekilde geri gelecektir.”
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Bundan sonra elçiler, Yeruşalim'den yaklaşık bir kilometre uzaklıktaki Zeytin Dağı'ndan Yeruşalim'e döndüler.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 Kente girince kaldıkları evin üst katındaki odaya çıktılar. Petrus, Yuhanna, Yakup, Andreas, Filipus, Tomas, Bartalmay, Matta, Alfay oğlu Yakup, Yurtsever Simun ve Yakup oğlu Yahuda oradaydı.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 Bunlar İsa'nın annesi Meryem, öbür kadınlar ve İsa'nın kardeşleriyle tam bir birlik içinde sürekli dua ediyordu.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 O günlerde Petrus, yaklaşık yüz yirmi kardeşten oluşan bir topluluğun ortasında ayağa kalkıp şöyle konuştu: “Kardeşler, Kutsal Ruh'un, İsa'yı tutuklayanlara kılavuzluk eden Yahuda ile ilgili olarak Davut'un ağzıyla önceden bildirdiği Kutsal Yazı'nın yerine gelmesi gerekiyordu.
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 Yahuda bizden biri sayılmış ve bu hizmette yerini almıştı.”
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 Bu adam, yaptığı kötülüğün karşılığında aldığı ücretle bir tarla satın aldı. Sonra baş aşağı düştü, bedeni yarıldı ve bütün bağırsakları dışarı döküldü.
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 Yeruşalim'de yaşayan herkes olayı duydu. Tarlaya kendi dillerinde Kan Tarlası anlamına gelen Hakeldema adını verdiler.
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 “Nitekim Mezmurlar Kitabı'nda şöyle yazılmıştır” dedi Petrus. “‘Onun konutu ıssız kalsın, İçinde oturan olmasın.’ Ve, ‘Onun görevini bir başkası üstlensin.’
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 “Buna göre, Yahya'nın vaftiz döneminden başlayarak Rab İsa'nın aramızdan yukarı alındığı güne değin bizimle birlikte geçirdiği bütün süre boyunca yanımızda bulunan adamlardan birinin, İsa'nın dirilişine tanıklık etmek üzere bize katılması gerekir.”
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 Böylece iki kişiyi, Barsabba denilen ve Yustus diye de bilinen Yusuf ile Mattiya'yı önerdiler.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 Sonra şöyle dua ettiler: “Ya Rab, sen herkesin yüreğini bilirsin. Yahuda'nın, ait olduğu yere gitmek için bıraktığı bu hizmeti ve elçilik görevini üstlenmek üzere bu iki kişiden hangisini seçtiğini göster bize.”
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 Ardından bu iki kişiye kura çektirdiler; kura Mattiya'ya düştü. Böylelikle Mattiya on bir elçiye katıldı.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

< Elçilerin İşleri 1 >