< 2 Petrus 2 >

1 Ama İsrail halkı arasında sahte peygamberler vardı; tıpkı sizin de aranızda yanlış öğreti yayanlar olacağı gibi. Bunlar kendilerini satın alan Efendi'yi bile yadsıyarak gizlice aranıza yıkıcı öğretiler sokacaklar. Böyleleri kendi başlarına ani bir yıkım getirecek.
Koma panalinso aneneri onama pakati pa Aisraeli, monga padzakhalanso aphunzitsi onyenga pakati panu. Iwo adzalowetsa mwamseri ziphunzitso zonama ndi zowononga, nadzakana Ambuye amene anawawombola, ndipo motero adzadziyitanira okha chiwonongeko mwadzidzidzi.
2 Birçokları da onların sefahatine kapılacak. Onların yüzünden gerçeğin yoluna sövülecek.
Ambiri adzatsata njira zawo zochititsa manyazi ndipo chifukwa cha iwowa, anthu adzanyoza njira ya choonadi.
3 Açgözlülüklerinden ötürü uydurma sözlerle sizi sömürecekler. Onlar için çoktan beri verilmiş olan yargı gecikmez. Onları bekleyen yıkım da uyuklamaz.
Pofuna kupeza chuma, aphunzitsiwa adzakudyerani chuma chanu pokuwuzani nkhani zopeka. Chiweruzo chawo chinakonzedwa kale, ndipo chikuwadikira.
4 Tanrı günah işleyen melekleri esirgemedi; onları cehenneme atıp karanlıkta zincire vurdu. Yargılanıncaya dek orada tutulacaklar. (Tartaroō g5020)
Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō g5020)
5 Tanrı eski dünyayı da esirgemedi. Ama tanrısızların dünyasına tufanı gönderdiğinde, doğruluk yolunu bildiren Nuh'u ve yedi kişiyi daha korudu.
Iye sanalekerere dziko lapansi kalelo, koma anapulumutsa Nowa, mlaliki wa chilungamo, ndi anthu ena asanu ndi awiri atadzetsa chigumula pa dziko lapansi kwa anthu akhalidwe losapembedza Mulunguyo.
6 Sodom ve Gomora kentlerini yakıp yıkarak yargıladı. Böylece tanrısızların başına geleceklere bir örnek verdi.
Mulungu anaweruza mizinda ya Sodomu ndi Gomora nayiwononga ndi moto, kuti ikhale chitsanzo cha zimene zidzachitikira anthu osapembedza Mulungu.
7 Ama ilke tanımayan kişilerin sefih yaşayışından azap duyan doğru adam Lut'u kurtardı.
Koma Iye anapulumutsa Loti, munthu wolungama, amene ankavutika ndi khalidwe lonyansa la anthu oyipa.
8 Çünkü onların arasında yaşayan bu doğru adam, görüp işittiği yasa tanımaz davranışlar yüzünden doğru yüreğinde her gün ıstırap çekerdi.
(Pakuti munthu wolungamayo, pokhala pakati pawo tsiku ndi tsiku ankavutika mu mtima ndi makhalidwe awo oyipa amene ankawaona ndi kuwamva).
9 Görülüyor ki Rab kendi yolunda yürüyenleri karşılaştıkları denemelerden nasıl kurtaracağını bilir. Doğru olmayanları, özellikle benliğin yozlaşmış tutkuları ardından giden ve yetkisini hor görenleri cezalandırarak yargı gününe dek nasıl alıkoyacağını da bilir. Bu küstah, dikbaşlı kişiler yüce varlıklara sövmekten korkmazlar.
Tsono mutha kuona kuti Ambuye amadziwa kuwapulumutsa kwake pa mayesero anthu opembedza. Amadziwanso kusunga osalungama kuti alangidwe mpaka tsiku la chiweruzo.
Makamaka amene amatsata zilakolako zonyansa zathupi nanyoza ulamuliro. Anthu amenewa ndi odzikuza, ndipo otsata chifuniro cha iwo eni, sasamala za munthu, saopa kuchitira chipongwe zolengedwa za mmwamba.
11 Oysa melekler bile, güç ve kudrette daha üstün oldukları halde bu varlıkları Rab'bin önünde söverek yargılamazlar.
Komatu ngakhale angelo, amene ali akulu ndi amphamvu kuwaposa, sayankhula za chipongwe pobweretsa chiweruzo pa iwo kuchokera kwa Ambuye.
12 Ama anlamadıkları konularda sövüp sayan bu kişiler, içgüdüleriyle yaşayan, yakalanıp boğazlanmak üzere doğan, akıldan yoksun hayvanlar gibidir. Hayvanlar gibi onlar da yıkıma uğrayacaklar.
Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ali ngati zirombo zopanda nzeru. Zirombo zolengedwa kuti zigwidwe ndi kuwonongedwa, ndipo ngati zirombozo adzawonongedwa.
13 Ettikleri haksızlığa karşılık zarar görecekler. Gündüzün zevk alemlerine dalmayı eğlence sayarlar. Birer leke ve yüzkarasıdırlar. Sizinle yiyip içerken kendi hilelerinden zevk alırlar.
Iwo adzalangidwa chifukwa cha zoyipa zimene anachita. Koma chimene chimawakomera ndi kumangochita zokondweretsa thupi masanasana. Iwo ali ngati mawanga ndi zilema. Podya nanu pamodzi amakondwera kuchita za chinyengo.
14 Gözleri zinayla doludur, günaha doymazlar. Kararsız kişileri ayartırlar. Yüreği açgözlülüğe alıştırılmış lanetli insanlardır.
Ndi maso awo odzaza ndi chigololo, salekeza kuchimwa. Amanyengerera anthu osakhazikika. Iwo ndi akatswiri pa dyera ndi chuma, ndipo ndi ana otembereredwa!
15 Haksızlıkla elde ettiği kazancı seven Beor oğlu Balam'ın yolunu tutarak doğru yolu bırakıp saptılar.
Iwo anasiya njira yolungama ndipo anapatuka kutsata njira ya Baalamu mwana wa Beori, amene anakonda malipiro a chosalungama.
16 Balam işlediği suçtan ötürü azarlandı. Konuşamayan eşek, insan diliyle konuşarak bu peygamberin çılgınlığına engel oldu.
Koma anadzudzulidwa chifukwa cha kulakwa kwakeko. Bulu, nyama imene siyankhula, inayankhula ngati munthu kuletsa misala ya mneneriyo.
17 Bu kişiler, susuz pınarlar, fırtınanın dağıttığı sis gibidirler. Onları koyu karanlık bekliyor.
Anthu amenewa ali ngati akasupe wopanda madzi, ndiponso ngati nkhungu yowuluzidwa ndi mphepo yamkuntho. Mulungu wawasungira mdima wandiweyani.
18 Çünkü yanlış yolda yürüyenlerden henüz kurtulanları, boş ve kurumlu sözler söyleyerek benliğin tutkularıyla, sefahatle ayartırlar.
Pakuti anayankhula mawu opanda pake ndi onyada, ndipo ndi zilakolako zoyipa za thupi amanyenga anthu amene angopulumuka kumene pakati pa anzawo oyipa.
19 Onlara özgürlük vaat ederler, oysa kendileri yozlaşmışlığın kölesidirler. Çünkü insan neye yenilirse onun kölesi olur.
Amawalonjeza ufulu, pomwe iwo eni ndi akapolo a zizolowezi zowononga. Pajatu munthu amakhala kapolo wa chilichonse chimene chikumulamulira.
20 Rab ve Kurtarıcı İsa Mesih'i tanımakla dünyanın çirkefliğinden kurtulduktan sonra yine aynı işlere karışıp yenilirlerse, son durumları ilk durumlarından beter olur.
Ngati anapulumuka ku zodetsa za dziko lapansi podziwa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu, pambuyo pake nagwidwanso ndi kugonjetsedwa ndi zomwezo, potsiriza adzakhala oyipa kuposa mmene analili poyamba.
21 Çünkü doğruluk yolunu bilip de kendilerine emanet edilen kutsal buyruktan geri dönmektense, bu yolu hiç bilmemiş olmak onlar için daha iyi olurdu.
Kukanakhala bwino akanapanda kudziwa njira ya chilungamo, koposa ndi kuyileka atadziwa lamulo loyera limene Mulungu anawapatsa.
22 Şu gerçek özdeyiş onların durumunu anlatıyor: “Köpek kendi kusmuğuna döner”, “Domuz da yıkandıktan sonra çamurda yuvarlanmaya döner.”
Kwa iwo miyambi iyi ndi yoona, “Galu wabwerera ku masanzi ake,” ndipo, “Nkhumba imene inasamba, yakunkhunizikanso mʼmatope.”

< 2 Petrus 2 >