< 2 Krönikeboken 35 >

1 Och Josia höll Herranom Passah i Jerusalem; och slagtade Passah på fjortonde dagenom i första månaden.
Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
2 Och han ställde Presterna uti deras vakt, och styrkte dem till deras ämbete i Herrans hus;
Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
3 Och sade till Leviterna, som hela Israel lärde, och Herranom helgade voro: Låter den helga arken uti huset, som Salomo, Davids son, Israels Konung, byggt hafver; I skolen icke bära honom på axlarna; så tjener nu Herranom edrom Gud, och hans folke Israel;
Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
4 Och skicker edra fäders hus, i edor skifte, såsom de beskrifne äro af David, Israels Konung, och hans son Salomo.
Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
5 Och står i helgedomenom efter fädernas hus skifte ibland edra bröder af folket, och desslikes fädernas hus skifte ibland Leviterna.
“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
6 Och slagter Passah, och helger eder, och skicker edra bröder, att de göra efter Herrans ord genom Mose.
Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
7 Och Josia gaf till häfoffer för den meniga man lamb och kid, alltsammans till Passah, för alla dem som vid handena voro, på talet tretiotusend, och tretusend nöt; alltsammans af Konungens ägodelar.
Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
8 Hans Förstar gåfvo till häfoffer friviljoge för folket, och för Presterna och Leviterna; nämliga Hilkia, Sacharia och Jehiel, Förstarna i Guds hus, ibland Presterna till Passah, tutusend och sexhundrad ( lamb och kid ), dertill trehundrad nöt.
Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
9 Men Chanania, Semaja, Nethaneel, och hans bröder, Hasabia, Jejel och Josabad öfverstar för Leviterna, gåfvo Levitomen häfoffer till Passah, femtusend ( lamb och kid ), och dertill femhundrad nöt.
Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
10 Alltså vardt Gudstjenst beskickad, och Presterna stodo i sitt rum, och Leviterna i sin ordning, efter Konungens bud.
Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
11 Och de slagtade Passah, och Presterna togo af deras händer och stänkte, och Leviterna drogo thy hudena af;
Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
12 Och gjorde bränneoffer deraf, att de skulle dela det ut ibland fädershusen uti deras meniga hop, till att offrat Herranom, såsom skrifvet står i Mose bok; sammaledes gjorde de ock med oxarna.
Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
13 Och de kokade Passah vid eld, såsom det sig borde; men hvad som helgadt var, kokade de i grytor, kettlar och pannor, och de gjorde det med hast för meniga hopen.
Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
14 Derefter redde de ock för sig, och för Presterna; förty Presterna, Aarons söner, hade att skaffa med bränneoffret, och med det feta, allt intill nattena; derföre måste Leviterna tillreda för sig och för Presterna, Aarons söner.
Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
15 Och sångarena, Assaphs barn, stodo i sitt rum, efter Davids bud, och Assaphs, och Hemans, och Jeduthuns, Konungens Siares; och dörravaktarena vid alla dörrarna, och de veko intet ifrå sitt ämbete; ty Leviterna, deras bröder, redde till för dem.
Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
16 Alltså vardt beskickad all Herrans tjenst på den dagen, så att man höll Passah, och bränneoffer gjorde på Herrans altare, efter Konung Josia bud.
Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
17 Alltså höllo Israels barn, som vid handen voro, Passah i den tiden, och osyrade bröds högtid i sju dagar.
Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Intet Passah var i Israel hållet, såsom detta, allt ifrå den Propheten Samuels tid; och ingen Israels Konung hade sådant Passah hållit, såsom Josia Passah höll, och Presterna, Leviterna, hela Juda och det af Israel för handen var, och Jerusalems inbyggare.
Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
19 Uti adertonde årena af Josia rike vardt detta Passah hållet.
Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
20 Derefter, när Josia huset tillredt hade, drog Necho, Konungen i Egypten, upp, till att strida emot Carchemis vid Phrath; och Josia drog ut emot honom.
Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
21 Men han sände båd till honom, och lät säga honom: Hvad hafver jag med dig göra, Juda Konung? Jag kommer icke nu emot dig, utan jag strider emot ett ( annat ) hus; och Gud hafver sagt, att jag skulle skynda mig; håll upp att göra emot Gud, som med mig är, att han icke förderfvar dig.
Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
22 Men Josia vände icke sitt ansigte ifrå honom, utan ställde sig till att strida emot honom; och lydde intet Necho ord utaf Guds mun, och kom till att strida med honom på den slättene vid Megiddo.
Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
23 Och skyttorna sköto Konung Josia. Och Konungen sade till sina tjenare: Förer mig hädan; ty jag är illa sår.
Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
24 Och hans tjenare togo honom af vagnen, och lade honom på hans andra vagn, och förde honom till Jerusalem. Och han blef död, och vardt begrafven ibland sina fäders grifter; och hele Juda och Jerusalem sörjde för Josia skull.
Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
25 Och Jeremia jämrade sig öfver Josia; och alle sångare och sångerskor höllo deras klagovisor öfver Josia, allt intill denna dag, och gjorde en sedvänjo deraf i Israel; si, det är skrifvet uti de klagovisor.
Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
26 Hvad nu mer af Josia sägande är, och om hans barmhertighet, efter skriftene i Herrans lag,
Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
27 Och hans gerningar, både de första och de sista, si, det är skrifvet uti Israels och Juda Konungars bok.
zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

< 2 Krönikeboken 35 >