< Isaías 54 >

1 Que tu voz sea fuerte en la canción, oh mujer sin hijos; haz melodía y sonidos de alegría, tú que no has dado a luz; porque los hijos de ella que no tuvo marido son más que los de la esposa casada, dice el Señor.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Amplía el lugar de tu tienda, y extiende las cortinas de tu casa sin límites; haz que tus cuerdas se alarguen y tus estacas de tienda sean fuertes.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Porque ampliaré tus límites en la mano derecha y en la izquierda; y tu simiente tomará a las naciones como herencia, y hará que los pueblos llenos de gente sean desiertos.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 No tengas miedo; porque no quedarás humillada ni te quedarás sin esperanza; no te avergüences, porque la vergüenza de tu juventud se te borrará de la memoria y ya no tendrás en cuenta las tristezas de tus años viudos.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Porque tu Creador es tu marido; el señor de los ejércitos es su nombre, y el Santo de Israel es tu libertador; Será nombrado el Dios de toda la tierra.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Porque el Señor te ha hecho volver a él, como una esposa joven que ha sido expulsada y afligida de espíritu; como esposa joven que ha sido repudiada, pero tu Dios te ha vuelto a llamar y te dice.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 Por un corto tiempo te abandoné; Pero con gran misericordia te volveré a unir conmigo.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 En ira desbordante, mi rostro estuvo oculto de ti por un momento, pero te tendré compasión para siempre, dice el Señor tu redentor.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 Porque esto es como los días de Noé para mí, porque como hice un juramento de que las aguas de Noé nunca volverían a pasar sobre la tierra; también he jurado que no volveré a enojarme contigo, ni te reprenderé.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Porque las montañas pueden ser quitadas, y las colinas pueden ser removidas de sus lugares, pero mi amor no te será quitado, o mi acuerdo de paz se romperá, dice el Señor, quien ha tenido misericordia de ti.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 ¡Oh, desdichada, azotada por la tormenta, sin consuelo! Mira, tus piedras estarán enmarcadas en colores claros y tus bases serán zafiros.
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 Haré tus torres de rubíes y tus puertas de carbuncos, y la pared que te rodea será de todo tipo de piedras preciosas.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Y todos tus constructores serán hechos sabios por el Señor; y grande será la paz de tus hijos.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Todos tus derechos te serán asegurados; no tengas miedo del mal, y la destrucción no se acercará a ti.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Mira, pueden ser movidos a la guerra, pero no por mi autoridad; todos los que se unan para atacarte, serán quebrantados contra ti.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Mira, he hecho al herrero, soplando las brasas y haciendo el instrumento de guerra por su trabajo; Y he creado al destructor para la destrucción.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Ningún instrumento de guerra que se forme contra ti será de ninguna utilidad; y toda lengua que dice mal contra ti, será juzgada como falsa. Esta es la herencia de los siervos del Señor, y su justicia viene de mí, dice el Señor.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.

< Isaías 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark