< Isaías 13 >

1 La palabra del Señor acerca de Babilonia que vio Isaías, el hijo de Amoz.
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Pon una bandera en la cima de una montaña, alza un grito fuerte, da instrucciones con la mano, para que puedan entrar por las puertas de los nobles.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 He dado órdenes a mis consagrados, he enviado a mis hombres de guerra, los míos que se enorgullecen de mi gloria, para que den efecto a mi ira.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 ¡El ruido de grandes números en las montañas, como el ruido de un pueblo fuerte! ¡El ruido de los reinos de las naciones reunidas! El señor de los ejércitos está ordenando sus fuerzas para la guerra.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 Vienen de un país lejano, de la parte más lejana del cielo, incluso el Señor y los instrumentos de su ira, con destrucción por toda la tierra.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Envía un grito de dolor; porque cerca está el día del Señor; viene como destrucción del Altísimo.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Por esta causa, todas las manos serán débiles, y todo corazón del hombre desfallecerá;
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Sus corazones estarán llenos de temor; Dolores y penas los vencerán; Estarán sufriendo como una mujer en el parto; se sorprenderán el uno del otro; sus rostros serán como llamas.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Mira, el día del Señor viene, cruel, con ira y ardiente furor; convertirá de la tierra un desierto, llevando a los pecadores a la destrucción.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Porque las estrellas del cielo y sus ejércitos brillantes no darán su luz: el sol se oscurecerá en su viaje por el cielo, y la luna retendrá su luz.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 Y enviaré castigo al mundo por su maldad, y a los pecadores por sus malas acciones; y pondré fin a todo orgullo, y abatiré el poder de los crueles.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Haré que los hombres sean tan pequeños en número, que un hombre será más difícil de conseguir que el oro, incluso el mejor oro de Ofir.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Por esta causa temblarán los cielos, y la tierra se moverá de su lugar, en la ira del Señor de los ejércitos, y en el día del furor de mi ira.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 Y será que, como una gacela huyendo, y como ovejas errantes, irán cada uno a su pueblo y a su tierra.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Todos los que sean adelantados tendrán una lanza atravesada por él, y todos los que huyan serán arrojados a la espada.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Sus hijos pequeños serán estrellados contra el suelo delante de sus ojos; sus bienes serán saqueados, y sus esposas serán violadas.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Mira, estoy manejando a los medos contra ellos, que no le dan valor a la plata y no tienen placer en el oro.
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 En sus manos hay arcos y lanzas; son crueles, matan violentamente a los jóvenes y aplastan a los recién nacidos; no tienen piedad por los niños.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Y Babilonia, la gloria de los reinos, la hermosa ciudad que es el orgullo de los caldeos, será como la destrucción de Dios de Sodoma y Gomorra.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 La gente nunca volverá a vivir en ella, y no tendrá más hombres de generación en generación: el árabe no levantará su tienda allí; y los que cuidan ovejas no lo harán un lugar de descanso para sus rebaños.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Pero las bestias del desierto tendrán sus agujeros allí; y las casas estarán llenas de lechuzas, y los avestruces tendrán su lugar allí, y los chivos retozaran allí.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Y los lobos se responderán unos a otros en sus torres fortificadas, y los chacales en sus lujosos palacios: su tiempo está cerca, y sus días de poder se terminarán rápidamente.
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

< Isaías 13 >