< 2 Reyes 1 >

1 Después de la muerte de Acab, Moab se rebeló contra Israel.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 Entonces Ocozías se cayó de la ventana de su habitación en Samaria y estaba enfermo. Y envió a los hombres, y les dijo: Haz una pregunta a Baal-zebub, el dios de Ecrón, sobre el resultado de mi enfermedad, para ver si estoy bien o no.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Pero el ángel del Señor le dijo a Elías el Tisbe: Ve ahora, a encuentro con los hombres enviados por el rey de Samaria, pregunta: ¿Es porque no hay Dios en Israel, que vas? para obtener direcciones de Baal-zebub, el dios de Ecrón?
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Escucha las palabras del Señor: Nunca más volverás a bajar de la cama a la que has subido, pero la muerte sin duda te llegará. Entonces Elías se fue.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Y los hombres que había enviado regresaron al rey; Y él les preguntó: ¿Por qué han vuelto?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Y le dijeron: En nuestro camino tuvimos una reunión con un hombre que dijo: Vuelve al rey que te envió y dile: El Señor dice: ¿Acaso no hay Dios en Israel? ¿Que envías para hacerle una pregunta a Baal-zebub, el dios de Ecrón? Por esta razón, no te levantarás de la cama en la que te has acostado, pero la muerte sin duda te llegará.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Y él les dijo: ¿Qué clase de hombre fue quien vino y les dijo estas palabras?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 Y ellos respondieron: Era un hombre velludo, con una banda de cuero alrededor de su cuerpo. Entonces él dijo: Es Elías el Tisbe.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Entonces el rey le envió un capitán de cincuenta con sus cincuenta hombres; y subió a él donde estaba sentado en la cima de una colina, y le dijo: Oh hombre de Dios, el rey ha dicho: Desciende.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 Y Elías, en respuesta, dijo al capitán de los cincuenta: Si soy hombre de Dios, que el fuego descienda del cielo sobre ti y sobre tus cincuenta hombres, y te ponga fin. Entonces el fuego bajó del cielo y puso fin a él y a sus cincuenta hombres.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Entonces el rey envió a otro capitán de cincuenta con sus cincuenta hombres; Y dijo a Elías: Oh hombre de Dios, el rey dice: Desciende pronto.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 Y Elías, en respuesta, dijo: Si soy hombre de Dios, que descienda fuego del cielo sobre ti y sobre tus cincuenta hombres, y te ponga fin. Y el fuego de Dios descendió del cielo y puso fin a él y a sus cincuenta hombres.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Entonces envió a un tercer capitán de cincuenta con sus cincuenta hombres; y el tercer capitán de los cincuenta subió, y, arrodillado ante Elías, pidiendo misericordia de él, dijo: Oh hombre de Dios, deja que mi vida y la vida de estos tus cincuenta siervos te sean de valor.
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Porque el fuego bajó del cielo y puso fin a los dos primeros capitanes de los cincuenta y a sus hombres; Pero ahora deja que mi vida sea de valor en tus ojos.
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 Entonces el ángel del Señor dijo a Elías: Desciende con él; No le tengas miedo. Entonces se levantó y descendió con él al rey.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 Y él le dijo: Esta es la palabra del Señor: Porque enviaste a los hombres a hacerle una pregunta a Baal-zebub, el dios de Ecrón, como si en Israel no hubiera Dios, por esta razón nunca más volverás a bajar de la cama. a lo que has subido, pero la muerte ciertamente vendrá a ti.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 Y vino a él la muerte, como el Señor había dicho por boca de Elías. Y Joram se hizo rey en su lugar en el segundo año del gobierno de Joram, hijo de Josafat, rey de Judá; porque nunca tuvo hijos.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Los demás hechos de Ocozías, ¿no están registrados en el libro de la historia de los reyes de Israel?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< 2 Reyes 1 >