< 1 Reyes 15 >

1 En el año dieciocho del rey Jeroboam, hijo de Nabat, Abiam se convirtió en rey de Judá.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Durante tres años reinó en Jerusalén, y el nombre de su madre fue Maaca, hija de Absalón.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 E hizo los mismos pecados que su padre había hecho antes que él: su corazón no era completamente fiel al Señor su Dios, como el corazón de David su padre.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Pero a causa de David, el Señor le dio una luz en Jerusalén, haciendo reyes a sus hijos después de él, para que Jerusalén estuviera a salvo;
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Porque David hizo lo correcto ante los ojos del Señor, y nunca en toda su vida fue en contra de sus órdenes, sino solo en la cuestión de Urías el hitita.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 Hubo guerra continua entre Roboam y Jeroboam.
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Los demás hechos de Abiam y todo lo que hizo, ¿no están registrados en el libro de las crónicas de los reyes de Judá? Y hubo guerra entre Abiam y Jeroboam.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Entonces Abiam fue a dormir con sus padres, y lo enterraron en el pueblo de David: y Asa su hijo se convirtió en rey en su lugar.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 En el año veinte en que Jeroboam era rey de Israel, Asa se convirtió en rey de Judá.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 Y reinó en Jerusalén durante cuarenta y un años; El nombre de su madre era Maaca, la hija de Absalón.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Asa hizo lo correcto ante los ojos del Señor, como lo hizo David su padre.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 También expulsó aquellos utilizados con fines sexuales en la adoración de los dioses, él los echó fuera del país, y quitó todas las imágenes que sus padres habían hecho.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Y él no permitiría que su madre Maaca fuera reina, porque ella había hecho una imagen repugnante para Asera; y Asa hizo cortar la imagen y quemarla en el arroyo Cedrón.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 Los lugares altos, sin embargo, no fueron quitados, pero aún así el corazón de Asa fue fiel al Señor toda su vida.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 Tomó en la casa del Señor todas las cosas que su padre había santificado, y las que él mismo había santificado, plata, oro y vasos.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Y hubo guerra entre Asa y Baasa, rey de Israel, todos los días.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Y Baasa, rey de Israel, subió contra Judá, fortificó a Ramá, para que nadie pudiera salir ni entrar a Asa, rey de Judá.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Entonces Asa tomó toda la plata y el oro que todavía estaban almacenados en la casa del Señor y en la casa del rey, y los envió, al cuidado de sus siervos, a Ben Adad, hijo de Tabrimon, hijo de Hezion, rey de Aram, en Damasco, diciendo:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 Hágase un acuerdo entre usted y yo, como hubo entre mi padre y su padre: mira, les he enviado una ofrenda de plata y oro; Ve y pon fin a tu acuerdo con Baasa, rey de Israel, para que pueda dejar de atacarme.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 Entonces Ben-adad hizo como dijo el rey Asa, y envió a los capitanes de sus ejércitos contra las ciudades de Israel, atacando a Ijon y Dan y Abel-bet-maaca, y a todos los Cineret en toda la tierra de Neftalí.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Baasa, al oírlo, dejó de fortificar Ramá y se quedó en Tirsa.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Entonces el rey Asa reunió a toda Judá, haciendo que todos vinieran; y se llevaron las piedras y la madera con que Baasa estaba construyendo a Ramá, y el rey Asa las utilizó para construir a Geba en la tierra de Benjamín y Mizpa.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Los demás hechos de Asa, y su poder, y todo lo que hizo, y los pueblos de los cuales fue el constructor, ¿no están registrados en el libro de las crónicas de los reyes de Judá? Más cuando era viejo tenía una enfermedad de los pies.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 Y cuando durmió Asa fue enterrado con sus antepasados en la ciudad de David, su padre; y Josafat su hijo se convirtió en rey en su lugar.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Nadab, hijo de Jeroboam, se convirtió en rey de Israel en el segundo año que Asa rey de Judá; y él fue rey de Israel por dos años.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 Él hizo lo malo ante los ojos del Señor, copiando los caminos malos de su padre, y en el pecado que hizo pecar a Israel.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 Y Baasa, hijo de Ahías, de la familia de Isacar, hizo un plan secreto contra él, atacándolo en Gibeton, un pueblo de los filisteos; porque Nadab y los ejércitos de Israel estaban haciendo la guerra a Gibeton.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 En el tercer año del gobierno de Asa, rey de Judá, Baasa lo mató y se convirtió en rey en su lugar.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Enseguida, cuando llegó a ser rey, envió destrucción a toda la descendencia de Jeroboam; No había una sola persona viva de toda la familia de Jeroboam a quien no matara, de modo que vino la palabra del Señor, que dijo por su siervo Ahías de Silo;
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 A causa de los pecados que hizo Jeroboam e hizo que Israel lo hiciera, moviendo al Señor, el Dios de Israel, a la ira.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Los demás hechos de Nadab y todo lo que hizo, ¿no están registrados en el libro de las crónicas de los reyes de Israel?
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 Y hubo guerra entre Asa y Baasa, rey de Israel, todos sus días.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 En el tercer año del gobierno de Asa, rey de Judá, Baasa, hijo de Ahías, se convirtió en rey de todo Israel en Tirsa, y fue rey durante veinticuatro años.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 Él hizo lo malo ante los ojos del Señor, copiando los caminos malos de Jeroboam y el pecado que hizo que Israel hiciera.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.

< 1 Reyes 15 >