< Cantar de los Cantares 1 >

1 CANCIÓN de canciones, la cual es de Salomón.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 ¡Oh si él me besara con ósculos de su boca! porque mejores son tus amores que el vino.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Por el olor de tus suaves ungüentos, (ungüento derramado es tu nombre, ) por eso las doncellas te amaron.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Llévame en pos de ti, correremos. Metióme el rey en sus cámaras: nos gozaremos y alegraremos en ti; acordarémonos de tus amores más que del vino: los rectos te aman.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Morena soy, oh hijas de Jerusalem, mas codiciable; como las cabañas de Cedar, como las tiendas de Salomón.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 No miréis en que soy morena, porque el sol me miró. Los hijos de mi madre se airaron contra mí, hiciéronme guarda de viñas; [y] mi viña, que era mía, no guardé.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Hazme saber, ó tú á quien ama mi alma, dónde repastas, dónde haces tener majada al medio día: porque, ¿por qué había yo de estar como vagueando tras los rebaños de tus compañeros?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 Si tú no lo sabes, oh hermosa entre las mujeres, sal, yéndote por las huellas del rebaño, y apacienta tus cabritas junto á las cabañas de los pastores.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 A yegua de los carros de Faraón te he comparado, amiga mía.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Hermosas son tus mejillas entre los pendientes, tu cuello entre los collares.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Zarcillos de oro te haremos, con clavos de plata.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 Mientras que el rey estaba en su reclinatorio, mi nardo dió su olor.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Mi amado es para mí un manojito de mirra, que reposa entre mis pechos.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Racimo de copher en las viñas de Engadi es para mí mi amado.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 He aquí que tú eres hermosa, amiga mía; he aquí que eres bella: tus ojos de paloma.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 He aquí que tú eres hermoso, amado mío, y suave: nuestro lecho también florido.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 Las vigas de nuestra casa son de cedro, [y] de ciprés los artesonados.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Cantar de los Cantares 1 >