< Salmos 9 >

1 Al Músico principal: sobre Muth-labben: Salmo de David. TE alabaré, oh Jehová, con todo mi corazón; contaré todas tus maravillas.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Alegraréme y regocijaréme en ti: cantaré á tu nombre, oh Altísimo;
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Por haber sido mis enemigos vueltos atrás: caerán y perecerán delante de ti.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Porque has hecho mi juicio y mi causa: sentástete en silla juzgando justicia.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Reprendiste gentes, destruiste al malo, raíste el nombre de ellos para siempre jamás.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Oh enemigo, acabados son para siempre los asolamientos; y las ciudades que derribaste, su memoria pereció con ellas.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Mas Jehová permanecerá para siempre: dispuesto ha su trono para juicio.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Y él juzgará el mundo con justicia; y juzgará los pueblos con rectitud.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Y será Jehová refugio al pobre, refugio para el tiempo de angustia.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 Y en ti confiarán los que conocen tu nombre; por cuanto tú, oh Jehová, no desamparaste á los que te buscaron.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Cantad á Jehová, que habita en Sión: noticiad en los pueblos sus obras.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Porque demandando la sangre se acordó de ellos: no se olvidó del clamor de los pobres.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Ten misericordia de mí, Jehová: mira mi aflicción [que padezco] de los que me aborrecen, tú que me levantas de las puertas de la muerte;
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 Porque cuente yo todas tus alabanzas en las puertas de la hija de Sión, [y] me goce en tu salud.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Hundiéronse las gentes en la fosa que hicieron; en la red que escondieron fué tomado su pie.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Jehová fué conocido [en] el juicio que hizo; en la obra de sus manos fué enlazado el malo. (Higaion, Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 Los malos serán trasladados al infierno, todas las gentes que se olvidan de Dios. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 Porque no para siempre será olvidado el pobre; ni la esperanza de los pobres perecerá perpetuamente.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Levántate, oh Jehová; no se fortalezca el hombre; sean juzgadas las gentes delante de ti.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Pon, oh Jehová, temor en ellos: conozcan las gentes que son no más que hombres. (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Salmos 9 >