< Salmos 82 >

1 Salmo de Asaph. DIOS está en la reunión de los dioses; en medio de los dioses juzga.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 ¿Hasta cuándo juzgaréis injustamente, y aceptaréis las personas de los impíos? (Selah)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Defended al pobre y al huérfano: haced justicia al afligido y al menesteroso.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Librad al afligido y al necesitado: libradlo de mano de los impíos.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 No saben, no entienden, andan en tinieblas: vacilan todos los cimientos de la tierra.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Yo dije: Vosotros sois dioses, é hijos todos vosotros del Altísimo.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Empero como hombres moriréis, y caeréis como cualquiera de los tiranos.
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Levántate, oh Dios, juzga la tierra: porque tú heredarás en todas las gentes.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

< Salmos 82 >