< Salmos 78 >

1 Masquil de Asaph. ESCUCHA, pueblo mío, mi ley: inclinad vuestro oído á las palabras de mi boca.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Abriré mi boca en parábola; hablaré cosas reservadas de antiguo:
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Las cuales hemos oído y entendido; que nuestros padres nos [las] contaron.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 No las encubriremos á sus hijos, contando á la generación venidera las alabanzas de Jehová, y su fortaleza, y sus maravillas que hizo.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 El estableció testimonio en Jacob, y pusó ley en Israel; la cual mandó á nuestros padres que la notificasen á sus hijos;
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 Para que [lo] sepa la generación venidera, y los hijos que nacerán; y [los que] se levantarán, [lo] cuenten á sus hijos;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 A fin de que pongan en Dios su confianza, y no se olviden de las obras de Dios, y guarden sus mandamientos:
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 Y no sean como sus padres, generación contumaz y rebelde; generación que no apercibió su corazón, ni fué fiel para con Dios su espíritu.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Los hijos de Ephraim armados, flecheros, volvieron [las espaldas] el día de la batalla.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 No guardaron el pacto de Dios, ni quisieron andar en su ley:
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Antes se olvidaron de sus obras, y de sus maravillas que les había mostrado.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Delante de sus padres hizo maravillas en la tierra de Egipto, en el campo de Zoán.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Rompió la mar, é hízolos pasar; é hizo estar las aguas como en un montón.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Y llevólos de día con nube, y toda la noche con resplandor de fuego.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Hendió las peñas en el desierto: y dióles á beber como de grandes abismos;
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Pues sacó de la peña corrientes, é hizo descender aguas como ríos.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Empero aun tornaron á pecar contra él, enojando en la soledad al Altísimo.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Pues tentaron á Dios en su corazón, pidiendo comida á su gusto.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Y hablaron contra Dios, diciendo: ¿Podrá poner mesa en el desierto?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 He aquí ha herido la peña, y corrieron aguas, y arroyos salieron ondeando: ¿podrá también dar pan? ¿aparejará carne á su pueblo?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Por tanto oyó Jehová, é indignóse: y encendióse el fuego contra Jacob, y el furor subió también contra Israel;
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Por cuanto no habían creído á Dios, ni habían confiado en su salud:
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 A pesar de que mandó á las nubes de arriba, y abrió las puertas de los cielos,
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 E hizo llover sobre ellos maná para comer, y dióles trigo de los cielos.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Pan de nobles comió el hombre: envióles comida á hartura.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Movió el solano en el cielo, y trajo con su fortaleza el austro.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 E hizo llover sobre ellos carne como polvo, y aves de alas como arena de la mar.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 E hízolas caer en medio de su campo, alrededor de sus tiendas.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Y comieron, y hartáronse mucho: cumplióles pues su deseo.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 No habían quitado de sí su deseo, aun estaba su vianda en su boca,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Cuando vino sobre ellos el furor de Dios, y mató los más robustos de ellos, y derribó los escogidos de Israel.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Con todo esto pecaron aún, y no dieron crédito á sus maravillas.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Consumió por tanto en nada sus días, y sus años en la tribulación.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Si los mataba, entonces buscaban á Dios; entonces se volvían solícitos en busca suya.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Y acordábanse que Dios era su refugio, y el Dios Alto su redentor.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Mas le lisonjeaban con su boca, y con su lengua le mentían:
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Pues sus corazones no eran rectos con él, ni estuvieron firmes en su pacto.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Empero él misericordioso, perdonaba la maldad, y no [los] destruía: y abundó para apartar su ira, y no despertó todo su enojo.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Y acordóse que eran carne; soplo que va y no vuelve.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 ¡Cuántas veces lo ensañaron en el desierto, lo enojaron en la soledad!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Y volvían, y tentaban á Dios, y ponían límite al Santo de Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 No se acordaron de su mano, del día que los redimió de angustia;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Cuando puso en Egipto sus señales, y sus maravillas en el campo de Zoán;
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Y volvió sus ríos en sangre, y sus corrientes, porque no bebiesen.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Envió entre ellos una mistura de moscas que los comían, y ranas que los destruyeron.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Dió también al pulgón sus frutos, y sus trabajos á la langosta.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Sus viñas destruyó con granizo, y sus higuerales con piedra;
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Y entregó al pedrisco sus bestias, y al fuego sus ganados.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Envió sobre ellos el furor de su saña, ira y enojo y angustia, con misión de malos ángeles.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Dispuso el camino á su furor; no eximió la vida de ellos de la muerte, sino que entregó su vida á la mortandad.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 E hirió á todo primogénito en Egipto, las primicias de las fuerzas en las tiendas de Châm.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Empero hizo salir á su pueblo como ovejas, y llevólos por el desierto, como un rebaño.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Y guiólos con seguridad, que no tuvieron miedo; y la mar cubrió á sus enemigos.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Metiólos después en los términos de su santuario, en este monte que ganó su mano derecha.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Y echó las gentes de delante de ellos, y repartióles una herencia con cuerdas; é hizo habitar en sus moradas á las tribus de Israel.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Mas tentaron y enojaron al Dios Altísimo, y no guardaron sus testimonios;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Sino que se volvieron, y se rebelaron como sus padres: volviéronse como arco engañoso.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Y enojáronlo con sus altos, y provocáronlo á celo con sus esculturas.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Oyólo Dios, y enojóse, y en gran manera aborreció á Israel.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Dejó por tanto el tabernáculo de Silo, la tienda [en que] habitó entre los hombres;
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Y dió en cautividad su fortaleza, y su gloria en mano del enemigo.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Entregó también su pueblo á cuchillo, y airóse contra su heredad.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 El fuego devoró sus mancebos, y sus vírgenes no fueron loadas en cantos nupciales.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Sus sacerdotes cayeron á cuchillo, y sus viudas no lamentaron.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Entonces despertó el Señor á la manera del que ha dormido, como un valiente que grita excitado del vino:
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 E hirió á sus enemigos en las partes posteriores: dióles perpetua afrenta.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Y desechó el tabernáculo de José, y no escogió la tribu de Ephraim;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Sino que escogió la tribu de Judá, el monte de Sión, al cual amó.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Y edificó su santuario á manera de eminencia, como la tierra que cimentó para siempre.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Y eligió á David su siervo, y tomólo de las majadas de las ovejas:
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 De tras las paridas lo trajo, para que apacentase á Jacob su pueblo, y á Israel su heredad.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Y apacentólos con entereza de su corazón; y pastoreólos con la pericia de sus manos.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Salmos 78 >