< Salmos 61 >

1 Al Músico principal: sobre Neginoth: Salmo de David. OYE, oh Dios, mi clamor; á mi oración atiende.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 Desde el cabo de la tierra clamaré á ti, cuando mi corazón desmayare: á la peña más alta que yo me conduzcas.
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 Porque tú has sido mi refugio, [y] torre de fortaleza delante del enemigo.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Yo habitaré en tu tabernáculo para siempre: estaré seguro bajo la cubierta de tus alas.
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Porque tú, oh Dios, has oído mis votos, has dado heredad á los que temen tu nombre.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Días sobre días añadirás al rey: sus años serán como generación y generación.
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Estará para siempre delante de Dios: misericordia y verdad prepara que lo conserven.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Así cantaré tu nombre para siempre, pagando mis votos cada día.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

< Salmos 61 >