< Salmos 121 >

1 Cántico gradual. ALZARÉ mis ojos á los montes, de donde vendrá mi socorro.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Mi socorro [viene] de Jehová, que hizo los cielos y la tierra.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 No dará tu pie al resbaladero; ni se dormirá el que te guarda.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 He aquí, no se adormecerá ni dormirá el que guarda á Israel.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Jehová es tu guardador: Jehová es tu sombra á tu mano derecha.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 El sol no te fatigará de día, ni la luna de noche.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Jehová te guardará de todo mal: él guardará tu alma.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Jehová guardará tu salida y tu entrada, desde ahora y para siempre.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Salmos 121 >