< Salmos 111 >

1 Aleluya. ALABARÉ á Jehová con todo el corazón, en la compañía y congregación de los rectos.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Grandes son las obras de Jehová; buscadas de todos los que las quieren.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Gloria y hermosura es su obra; y su justicia permanece para siempre.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Hizo memorables sus maravillas: clemente y misericordioso es Jehová.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Dió mantenimiento á los que le temen; para siempre se acordará de su pacto.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 El poder de sus obras anunció á su pueblo, dándole la heredad de las gentes.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Las obras de sus manos son verdad y juicio: fieles son todos sus mandamientos;
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Afirmados por siglo de siglo, hechos en verdad y en rectitud.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Redención ha enviado á su pueblo; para siempre ha ordenado su pacto: santo y terrible es su nombre.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 El principio de la sabiduría es el temor de Jehová: buen entendimiento tienen cuantos ponen aquéllos por obra: su loor permanece para siempre.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Salmos 111 >