< Proverbios 4 >

1 OID, hijos, la doctrina de un padre, y estad atentos para que conozcáis cordura.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Porque os doy buena enseñanza; no desamparéis mi ley.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Porque yo fuí hijo de mi padre, delicado y único delante de mi madre.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Y él me enseñaba, y me decía: Mantenga tu corazón mis razones, guarda mis mandamientos, y vivirás:
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Adquiere sabiduría, adquiere inteligencia; no te olvides ni te apartes de las razones de mi boca;
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 No la dejes, y ella te guardará; ámala, y te conservará.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Sabiduría ante todo: adquiere sabiduría: y ante toda tu posesión adquiere inteligencia.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Engrandécela, y ella te engrandecerá: ella te honrará, cuando tú la hubieres abrazado.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Adorno de gracia dará á tu cabeza: corona de hermosura te entregará.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Oye, hijo mío, y recibe mis razones; y se te multiplicarán años de vida.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Por el camino de la sabiduría te he encaminado, y por veredas derechas te he hecho andar.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Cuando anduvieres no se estrecharán tus pasos; y si corrieres, no tropezarás.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Ten el consejo, no lo dejes; guárdalo, porque eso es tu vida.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 No entres por la vereda de los impíos, ni vayas por el camino de los malos.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Desampárala, no pases por ella; apártate de ella, pasa.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Porque no duermen ellos, si no hicieren mal; y pierden su sueño, si no han hecho caer.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Porque comen pan de maldad, y beben vino de robos.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Mas la senda de los justos es como la luz de la aurora, que va en aumento hasta que el día es perfecto.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 El camino de los impíos es como la oscuridad: no saben en qué tropiezan.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Hijo mío, está atento á mis palabras; inclina tu oído á mis razones.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 No se aparten de tus ojos; guárdalas en medio de tu corazón.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Porque son vida á los que las hallan, y medicina á toda su carne.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Sobre toda cosa guardada guarda tu corazón; porque de él mana la vida.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Aparta de ti la perversidad de la boca, y aleja de ti la iniquidad de labios.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Tus ojos miren lo recto, y tus párpados en derechura delante de ti.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Examina la senda de tus pies, y todos tus caminos sean ordenados.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 No te apartes á diestra, ni á siniestra: aparta tu pie del mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbios 4 >