< Proverbios 31 >

1 PALABRAS del rey Lemuel; la profecía con que le enseñó su madre.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 ¿Qué, hijo mío? ¿y qué, hijo de mi vientre? ¿y qué, hijo de mis deseos?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 No des á las mujeres tu fuerza, ni tus caminos á lo que es para destruir los reyes.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 No es de los reyes, oh Lemuel, no es de los reyes beber vino, ni de los príncipes la cerveza.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 No sea que bebiendo olviden la ley, y perviertan el derecho de todos los hijos afligidos.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Dad la cerveza al desfallecido, y el vino á los de amargo ánimo:
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Beban, y olvídense de su necesidad, y de su miseria no más se acuerden.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Abre tu boca por el mudo, en el juicio de todos los hijos de muerte.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Abre tu boca, juzga justicia, y el derecho del pobre y del menesteroso.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Mujer fuerte, ¿quién la hallará? porque su estima sobrepuja largamente á [la de] piedras preciosas.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 El corazón de su marido está en ella confiado, y no tendrá necesidad de despojo.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Darále ella bien y no mal, todos los días de su vida.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Buscó lana y lino, y con voluntad labró de sus manos.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Fué como navío de mercader: trae su pan de lejos.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 Levantóse aun de noche, y dió comida á su familia, y ración á sus criadas.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Consideró la heredad, y compróla; y plantó viña del fruto de sus manos.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Ciñó sus lomos de fortaleza, y esforzó sus brazos.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Gustó que era buena su granjería: su candela no se apagó de noche.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Aplicó sus manos al huso, y sus manos tomaron la rueca.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Alargó su mano al pobre, y extendió sus manos al menesteroso.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 No tendrá temor de la nieve por su familia, porque toda su familia está vestida de ropas dobles.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Ella se hizo tapices; de lino fino y púrpura es su vestido.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Conocido es su marido en las puertas, cuando se sienta con los ancianos de la tierra.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Hizo telas, y vendió; y dió cintas al mercader.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Fortaleza y honor son su vestidura; y en el día postrero reirá.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Abrió su boca con sabiduría: y la ley de clemencia está en su lengua.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Considera los caminos de su casa, y no come el pan de balde.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Levantáronse sus hijos, y llamáronla bienaventurada; y su marido también la alabó.
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Muchas mujeres hicieron el bien; mas tú las sobrepujaste á todas.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Engañosa es la gracia, y vana la hermosura: la mujer que teme á Jehová, ésa será alabada.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Dadle el fruto de sus manos, y alábenla en las puertas sus hechos.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Proverbios 31 >