< Proverbios 29 >

1 EL hombre que reprendido endurece la cerviz, de repente será quebrantado; ni habrá [para él] medicina.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Cuando los justos dominan, el pueblo se alegra: mas cuando domina el impío, el pueblo gime.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 El hombre que ama la sabiduría, alegra á su padre: mas el que mantiene rameras, perderá la hacienda.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 El rey con el juicio afirma la tierra: mas el hombre de presentes la destruirá.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 El hombre que lisonjea á su prójimo, red tiende delante de sus pasos.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 En la prevaricación del hombre malo hay lazo: mas el justo cantará y se alegrará.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Conoce el justo la causa de los pobres: [mas] el impío no entiende sabiduría.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Los hombres escarnecedores enlazan la ciudad: mas los sabios apartan la ira.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Si el hombre sabio contendiere con el necio, que se enoje ó que se ría, no tendrá reposo.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Los hombres sanguinarios aborrecen al perfecto: mas los rectos buscan su contentamiento.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 El necio da suelta á todo su espíritu; mas el sabio al fin le sosiega.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Del señor que escucha la palabra mentirosa, todos sus ministros son impíos.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 El pobre y el usurero se encontraron: Jehová alumbra los ojos de ambos.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 El rey que juzga con verdad á los pobres, su trono será firme para siempre.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 La vara y la corrección dan sabiduría: mas el muchacho consentido avergonzará á su madre.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Cuando los impíos son muchos, mucha es la prevaricación; mas los justos verán la ruina de ellos.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Corrige á tu hijo, y te dará descanso, y dará deleite á tu alma.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Sin profecía el pueblo será disipado: mas el que guarda la ley, bienaventurado él.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 El siervo no se corregirá con palabras: porque entiende, mas no corresponde.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 ¿Has visto hombre ligero en sus palabras? más esperanza hay del necio que de él.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 El que regala á su siervo desde su niñez, á la postre será su hijo.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 El hombre iracundo levanta contiendas; y el furioso muchas veces peca.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 La soberbia del hombre le abate; pero al humilde de espíritu sustenta la honra.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 El aparcero del ladrón aborrece su vida; oirá maldiciones, y no [lo] denunciará.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 El temor del hombre pondrá lazo: mas el que confía en Jehová será levantado.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Muchos buscan el favor del príncipe: mas de Jehová [viene] el juicio de cada uno.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Abominación es á los justos el hombre inicuo; y abominación es al impío el de rectos caminos.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Proverbios 29 >