< Proverbios 27 >

1 NO te jactes del día de mañana; porque no sabes qué dará de sí el día.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Alábete el extraño, y no tu boca; el ajeno, y no tus labios.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Pesada es la piedra, y la arena pesa; mas la ira del necio es más pesada que ambas cosas.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Cruel es la ira, é impetuoso el furor; mas ¿quién parará delante de la envidia?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Mejor es reprensión manifiesta que amor oculto.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Fieles son las heridas del que ama; pero importunos los besos del que aborrece.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 El alma harta huella el panal de miel; mas al alma hambrienta todo lo amargo es dulce.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Cual ave que se va de su nido, tal es el hombre que se va de su lugar.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 El ungüento y el perfume alegran el corazón: y el amigo al hombre con el cordial consejo.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 No dejes á tu amigo, ni al amigo de tu padre; ni entres en casa de tu hermano el día de tu aflicción: mejor es el vecino cerca que el hermano lejano.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Sé sabio, hijo mío, y alegra mi corazón, y tendré qué responder al que me deshonrare.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 El avisado ve el mal, [y] escóndese; [mas] los simples pasan, [y] llevan el daño.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Quítale su ropa al que fió al extraño; y [al que fió] á la extraña, tómale prenda.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 El que bendice á su amigo en alta voz, madrugando de mañana, por maldición se le contará.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Gotera continua en tiempo de lluvia, y la mujer rencillosa, son semejantes:
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 El que pretende contenerla, arresta el viento: ó el aceite en su mano derecha.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Hierro con hierro se aguza; y el hombre aguza el rostro de su amigo.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 El que guarda la higuera, comerá su fruto; y el que guarda á su señor, será honrado.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Como un agua se parece á otra, así el corazón del hombre al otro.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 El sepulcro y la perdición nunca se hartan: así los ojos del hombre nunca están satisfechos. (Sheol h7585)
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
21 El crisol [prueba] la plata, y la hornaza el oro: y al hombre la boca del que lo alaba.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Aunque majes al necio en un mortero entre granos de trigo á pisón majados, no se quitará de él su necedad.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Considera atentamente el aspecto de tus ovejas; pon tu corazón á tus rebaños:
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 Porque las riquezas no son para siempre; ¿y [será] la corona para perpetuas generaciones?
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Saldrá la grama, aparecerá la hierba, y segaránse las hierbas de los montes.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 Los corderos para tus vestidos, y los cabritos para el precio del campo:
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 Y abundancia de leche de las cabras para tu mantenimiento, y para mantenimiento de tu casa, y para sustento de tus criadas.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

< Proverbios 27 >