< Proverbios 12 >

1 EL que ama la corrección ama la sabiduría: mas el que aborrece la reprensión, es ignorante.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 El bueno alcanzará favor de Jehová: mas él condenará al hombre de malos pensamientos.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 El hombre no se afirmará por medio de la impiedad: mas la raíz de los justos no será movida.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 La mujer virtuosa corona es de su marido: mas la mala, como carcoma en sus huesos.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 Los pensamientos de los justos son rectitud; [mas] los consejos de los impíos, engaño.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 Las palabras de los impíos son para acechar la sangre: mas la boca de los rectos los librará.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 [Dios] trastornará á los impíos, y no serán más: mas la casa de los justos permanecerá.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 Según su sabiduría es alabado el hombre: mas el perverso de corazón será en menosprecio.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Mejor es el que es menospreciado y tiene servidores, que el que se precia, y carece de pan.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 El justo atiende á la vida de su bestia: mas las entrañas de los impíos son crueles.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 El que labra su tierra, se hartará de pan: mas el que sigue los vagabundos es falto de entendimiento.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 Desea el impío la red de los malos: mas la raíz de los justos dará [fruto].
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 El impío es enredado en la prevaricación de sus labios: mas el justo saldrá de la tribulación.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 El hombre será harto de bien del fruto de su boca: y la paga de las manos del hombre le será dada.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 El camino del necio es derecho en su opinión: mas el que obedece al consejo es sabio.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 El necio luego al punto da á conocer su ira: mas el que disimula la injuria es cuerdo.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 El que habla verdad, declara justicia; mas el testigo mentiroso, engaño.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 Hay quienes hablan como [dando] estocadas de espada: mas la lengua de los sabios es medicina.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 El labio de verdad permanecerá para siempre: mas la lengua de mentira por un momento.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Engaño hay en el corazón de los que piensan mal: mas alegría en el de los que piensan bien.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Ninguna adversidad acontecerá al justo: mas los impíos serán llenos de mal.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Los labios mentirosos son abominación á Jehová: mas los obradores de verdad su contentamiento.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 El hombre cuerdo encubre la ciencia: mas el corazón de los necios publica la necedad.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 La mano de los diligentes se enseñoreará: mas la negligencia será tributaria.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 El cuidado congojoso en el corazón del hombre, lo abate; mas la buena palabra lo alegra.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 El justo hace ventaja á su prójimo: mas el camino de los impíos les hace errar.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 El indolente no chamuscará su caza: mas el haber precioso del hombre [es] la diligencia.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 En el camino de la justicia está la vida; y la senda de su vereda no es muerte.
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Proverbios 12 >