< Job 36 >

1 Y AÑADIÓ Eliú, y dijo:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Espérame un poco, y enseñarte he; porque todavía [tengo] razones en orden á Dios.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Tomaré mi noticia de lejos, y atribuiré justicia á mi Hacedor.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Porque de cierto no son mentira mis palabras; contigo [está] el que es íntegro en [sus] conceptos.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 He aquí que Dios es grande, mas no desestima á nadie: es poderoso en fuerza de sabiduría.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 No otorgará vida al impío, y á los afligidos dará su derecho.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 No quitará sus ojos del justo; antes bien con los reyes los pondrá en solio para siempre, y serán ensalzados.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Y si estuvieren prendidos en grillos, y aprisionados en las cuerdas de aflicción,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 El les dará á conocer la obra de ellos, y que prevalecieron sus rebeliones.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Despierta además el oído de ellos para la corrección, y díce[les] que se conviertan de la iniquidad.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Si oyeren, y [le] sirvieren, acabarán sus días en bien, y sus años en deleites.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Mas si no oyeren, serán pasados á cuchillo, y perecerán sin sabiduría.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Empero los hipócritas de corazón lo irritarán más, y no clamarán cuando él los atare.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Fallecerá el alma de ellos en su mocedad, y su vida entre los sodomitas.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Al pobre librará de su pobreza, y en la aflicción despertará su oído.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Asimismo te apartaría de la boca de la angustia á lugar espacioso, [libre] de todo apuro; y te asentará mesa llena de grosura.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Mas tú has llenado el juicio del impío, [en vez] de sustentar el juicio y la justicia.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Por lo cual [teme] que [en su] ira no te quite con golpe, el cual no puedas apartar de ti con gran rescate.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 ¿Hará él estima de tus riquezas, ni del oro, ni de todas las fuerzas del poder?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 No anheles la noche, en que desaparecen los pueblos de su lugar.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Guárdate, no tornes á la iniquidad; pues ésta escogiste más bien que la aflicción.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 He aquí que Dios es excelso con su potencia: ¿qué enseñador semejante á él?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 ¿Quién le ha prescrito su camino? ¿y quién [le] dirá: Iniquidad has hecho?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Acuérdate de engrandecer su obra, la cual contemplan los hombres.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Los hombres todos la ven; mírala el hombre de lejos.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 He aquí, Dios es grande, y nosotros no le conocemos; ni se puede rastrear el número de sus años.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 El reduce las gotas de las aguas, al derramarse la lluvia según el vapor;
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Las cuales destilan las nubes, goteando en abundancia sobre los hombres.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 ¿Quién podrá tampoco comprender la extensión de las nubes, y el sonido estrepitoso de su pabellón?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 He aquí que sobre él extiende su luz, y cobija [con ella] las raíces de la mar.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Bien que por esos medios castiga á los pueblos, á la multitud da comida.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Con las nubes encubre la luz, y mándale [no brillar], interponiendo [aquéllas].
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Tocante á ella anunciará [el trueno], su compañero, [que hay] acumulación de ira sobre el que se eleva.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >