< Job 26 >

1 Y RESPONDIÓ Job, y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 ¿En qué ayudaste al que no tiene fuerza? ¿has amparado al brazo sin fortaleza?
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 ¿En qué aconsejaste al que no tiene ciencia, y mostraste bien sabiduría?
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 ¿A quién has anunciado palabras, y cúyo es el espíritu que de ti sale?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 Cosas inanimadas son formadas debajo de las aguas, y los habitantes de ellas.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 El sepulcro es descubierto delante de él, y el infierno no tiene cobertura. (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 Extiende el aquilón sobre vacío, cuelga la tierra sobre nada.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Ata las aguas en sus nubes, y las nubes no se rompen debajo de ellas.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 El restriñe la faz de su trono, y sobre él extiende su nube.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 El cercó con término la superficie de las aguas, hasta el fin de la luz y las tinieblas.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Las columnas del cielo tiemblan, y se espantan de su reprensión.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 El rompe la mar con su poder, y con su entendimiento hiere la hinchazón [suya].
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Su espíritu adornó los cielos; su mano crió la serpiente tortuosa.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 He aquí, estas son partes de sus caminos: ¡mas cuán poco hemos oído de él! Porque el estruendo de sus fortalezas, ¿quién lo detendrá?
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Job 26 >