< Job 17 >

1 MI ALIENTO está corrompido, acórtanse mis días, y me está aparejado el sepulcro.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 No hay conmigo sino escarnecedores, en cuya acrimonia se detienen mis ojos.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Pon ahora, dame fianza para [litigar] contigo: ¿quién tocará ahora mi mano?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Porque [á éstos] has tú escondido su corazón de inteligencia: por tanto, no [los] ensalzarás.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 El que denuncia lisonjas á sus prójimos, los ojos de sus hijos desfallezcan.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 El me ha puesto por parábola de pueblos, y delante [de ellos] he sido como tamboril.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Y mis ojos se oscurecieron de desabrimiento, y mis pensamientos todos son como sombra.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Los rectos se maravillarán de esto, y el inocente se levantará contra el hipócrita.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 No obstante, proseguirá el justo su camino, y el limpio de manos aumentará la fuerza.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Mas volved todos vosotros, y venid ahora, que no hallaré entre vosotros sabio.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Pasáronse mis días, fueron arrancados mis pensamientos, los designios de mi corazón.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Pusieron la noche por día, y la luz se acorta delante de las tinieblas.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Si yo espero, el sepulcro es mi casa: haré mi cama en las tinieblas. (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 A la huesa tengo dicho: Mi padre eres tú; á los gusanos: Mi madre y mi hermana.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 ¿Dónde pues estará ahora mi esperanza? y mi esperanza ¿quién la verá?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 A los rincones de la huesa descenderán, y juntamente descansarán en el polvo. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >