< Job 16 >

1 Y RESPONDIÓ Job, y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Muchas veces he oído cosas como estas: consoladores molestos sois todos vosotros.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 ¿Tendrán fin las palabras ventosas? ó ¿qué te animará á responder?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 También yo hablaría como vosotros. Ojalá vuestra alma estuviera en lugar de la mía, que yo os tendría compañía en las palabras, y sobre vosotros movería mi cabeza.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 [Mas] yo os alentaría con mis palabras, y la consolación de mis labios apaciguaría [el dolor vuestro].
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Si hablo, mi dolor no cesa; y si dejo [de hablar], no se aparta de mí.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Empero ahora me ha fatigado: has tú asolado toda mi compañía.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Tú me has arrugado; testigo es mi flacura, que se levanta contra mí para testificar en mi rostro.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Su furor [me] destrizó, y me ha sido contrario: crujió sus dientes contra mí; contra mí aguzó sus ojos mi enemigo.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Abrieron contra mí su boca; hirieron mis mejillas con afrenta; contra mí se juntaron todos.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Hame entregado Dios al mentiroso, y en las manos de los impíos me hizo estremecer
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Próspero estaba, y desmenuzóme: y arrebatóme por la cerviz, y despedazóme, y púsome por blanco suyo.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Cercáronme sus flecheros, partió mis riñones, y no perdonó: mi hiel derramó por tierra.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Quebrantóme de quebranto sobre quebranto; corrió contra mí como un gigante.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Yo cosí saco sobre mi piel, y cargué mi cabeza de polvo.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Mi rostro está enlodado con lloro, y mis párpados entenebrecidos:
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 A pesar de no haber iniquidad en mis manos, y de haber sido mi oración pura.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 ¡Oh tierra! no cubras mi sangre, y no haya lugar á mi clamor.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Mas he aquí que en los cielos está mi testigo, y mi testimonio en las alturas.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Disputadores [son] mis amigos: [mas] á Dios destilarán mis ojos.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 ¡Ojalá pudiese disputar el hombre con Dios, como con su prójimo!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Mas los años contados vendrán, y yo iré el camino por donde no volveré.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >