< Salmos 87 >

1 Su cimiento es en montes de santidad.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 Ama Jehová las puertas de Sión, más que todas las moradas de Jacob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Cosas ilustres son dichas de ti, ciudad de Dios. (Selah)
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 Yo me acordaré de Rahab y de Babilonia, entre los que me conocen: he aquí Palestina, y Tiro, con Etiopía: este nació allá.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 Y de Sión se dirá: Este, y aquel es nacido en ella: y el mismo Altísimo la fortificará.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 Jehová contará, cuando se escribieren los pueblos: Este nació allí. (Selah)
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 Y cantores con músicos de flautas: todas mis fuentes estarán en ti.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

< Salmos 87 >