< Salmos 76 >

1 Dios es conocido en Judá: Dios, en Israel es grande su nombre.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 Y en Salem está su tabernáculo: y su habitación en Sión.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Allí quebró las saetas del arco: el escudo, y la espada, y la guerra. (Selah)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Ilustre eres tú, y fuerte, más que los montes de caza.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Los fuertes de corazón fueron despojados; durmieron su sueño, y nada hallaron en sus manos todos los varones fuertes.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 Por tu reprensión, o! Dios de Jacob, es adormecido el carro y el caballo.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Tú eres terrible, tú: ¿y quién parará delante de ti en comenzando tu ira?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Desde los cielos hiciste oír juicio: la tierra tuvo temor, y cesó,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 Cuando, o! Dios, te levantaste al juicio, para salvar a todos los mansos de la tierra. (Selah)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 Ciertamente la ira del hombre te confesará: los restos de las iras constreñirás.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Prometéd, y pagád a Jehová, vuestro Dios, todos los que estáis al rededor de él: traigan presentes al terrible.
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 El que quita el espíritu a los príncipes: terrible a los reyes de la tierra.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Salmos 76 >