< Salmos 120 >

1 A Jehová llamé estando en angustia; y él me respondió.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 Jehová, escapa mi alma del labio mentiroso: de la lengua engañosa.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 ¿Qué te dará a ti, o qué te añadirá la lengua engañosa?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Es como saetas de valiente agudas con brasas de enebros.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 ¡Ay de mí que peregrino en Mesec: habito con las tiendas de Cedar!
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Mucho se detiene mi alma con los que aborrecen la paz.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Yo soy pacífico; y cuando hablo, ellos guerrean.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Salmos 120 >