< Números 33 >

1 Estas son las partidas de los hijos de Israel, que salieron de la tierra de Egipto por sus escuadrones, por mano de Moisés y Aarón,
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Que Moisés escribió sus salidas por sus partidas por dicho de Jehová: y estas son sus partidas por sus salidas.
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 De Ramesses partieron el mes primero a los quince días del mes primero: el segundo día de la pascua salieron los hijos de Israel con mano alta a ojos de todos los Egipcios.
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 Enterrando los Egipcios los que Jehová había muerto de ellos, a todo primogénito; y habiendo Jehová hecho juicios en sus dioses.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Partieron pues los hijos de Israel de Ramesses, y asentaron campo en Socot.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Y partiendo de Socot asentaron en Etam, que es al cabo del desierto.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Y partiendo de Etam volvieron sobre Pihahirot, que es delante de Baal-sefón, y asentaron delante de Magdalo.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Y partiendo de Pihahirot pasaron por medio de la mar al desierto, y anduvieron camino de tres días por el desierto de Etam, y asentaron en Mara.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Y partiendo de Mara vinieron a Elim, donde había doce fuentes de aguas y setenta palmas; y asentaron allí.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Y partidos de Elim asentaron junto al mar Bermejo.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Y partidos del mar Bermejo asentaron en el desierto de Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Y partidos del desierto de Sin asentaron en Dafca.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 Y partidos de Dafca asentaron en Alús.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 Y partidos de Alús asentaron en Rafidim, donde el pueblo no tuvo aguas para beber.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Y partidos de Rafidim asentaron en el desierto de Sinaí.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Y partidos del desierto de Sinaí asentaron en Kibrot-hattaava.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Y partidos de Kibrot-hattaava asentaron en Jaserot.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Y partidos de Jaserot asentaron en Retma.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 Y partidos de Retma asentaron en Remmon-fares.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Y partidos de Remmon-fares asentaron en Lebna.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Y partidos de Lebna asentaron en Ressa.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 Y partidos de Ressa asentaron en Cealata.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Y partidos de Cealata asentaron en el monte de Sefer.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Y partidos del monte de Sefer asentaron en Harada.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Y partidos de Harada asentaron en Macelot.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 Y partidos de Macelot asentaron en Tahat.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Y partidos de Tahat asentaron en Tare.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Y partidos de Tare asentaron en Metca.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 Y partidos de Metca asentaron en Hesmona.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Y partidos de Hesmona asentaron en Moserot.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Y partidos de Moserot asentaron en Bene-jaacán.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Y partidos de Bene-jaacán asentaron en el monte de Guidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 Y partidos del monte de Guidgad asentaron en Jetebata.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Y partidos de Jetebata asentaron en Hebrona.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Y partidos de Hebrona asentaron en Asión-gaber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 Y partidos de Asión-gaber asentaron en el desierto de Zin, que es Cádes.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 Y partidos de Cádes asentaron en el monte de Hor en el fin de la tierra de Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Y subió Aarón el sacerdote en el monte de Hor, conforme al dicho de Jehová, y allí murió a los cuarenta años de la salida de los hijos de Israel de la tierra de Egipto, en el mes quinto, en el primero del mes.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Y era Aarón de edad de ciento y veinte y tres años cuando murió en el monte de Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Y oyó el Cananeo rey de Arad, que habitaba al mediodía en la tierra de Canaán, como habían entrado los hijos de Israel.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Y partidos del monte de Hor asentaron en Salmona.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Y partidos de Salmona asentaron en Funón.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Y partidos de Funón asentaron en Obot.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 Y partidos de Obot asentaron en Je-abarim en el término de Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Y partidos de Je-abarim asentaron en Dibon-gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 Y partidos de Dibon-gad asentaron en Helmon-deblataim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Y partidos de Helmon-deblataim asentaron en los montes de Abarim delante de Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 Y partidos de los montes de Abarim asentaron en los campos de Moab junto al Jordán de Jericó.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Finalmente asentaron junto al Jordán desde Bet-jesimot hasta Abel-satim en los campos de Moab.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 Y habló Jehová a Moisés en los campos de Moab junto al Jordán de Jericó, diciendo:
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Habla a los hijos de Israel, y díles: Cuando hubiereis pasado el Jordán a la tierra de Canaán,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 Echaréis a todos los moradores de la tierra de delante de vosotros, y destruiréis todas sus pinturas, y todas sus imágenes de fundición, destruiréis asimismo todos sus altos:
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 Y echaréis los moradores de la tierra, y habitaréis en ella: porque yo os la he dado para que la heredéis.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Y heredaréis la tierra por suertes por vuestras familias; al mucho daréis mucho por su heredad, y al poco daréis poco por su heredad: donde le saliere la suerte, allí la tendrá: por las tribus de vuestros padres heredaréis.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 Y si no echareis los moradores de la tierra de delante de vosotros, será, que los que dejareis de ellos serán por aguijones en vuestros ojos, y por espinas en vuestros costados, y afligiros han sobre la tierra en que vosotros habitareis.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 Y será, que como yo pensé hacerles a ellos, haré a vosotros.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Números 33 >