< Job 31 >

1 “Me prometí a mí mismo no mirar nunca con deseo a las jóvenes.
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 ¿Qué debe esperar la gente de Dios? ¿Qué recompensa debe darles el Todopoderoso en lo alto?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 ¿No es el desastre para los malvados y la destrucción para los que hacen el mal?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 ¿No ve Dios todo lo que hago, incluso cuenta cada paso que doy?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 ¿He vivido una vida engañosa? ¿He estado ansioso por decir mentiras?
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 ¡No! Que Dios me pese en la balanza de su justicia y que descubra mi integridad.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 “Si me he desviado del camino de Dios, si he dejado que lo que veo se convierta en mis deseos, si hay alguna mancha de pecado en mis manos,
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 entonces que otro coma lo que he sembrado, y que todo lo que he cultivado sea desarraigado.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Si una mujer me ha seducido, o si he buscado la oportunidad de acostarme con la mujer de mi prójimo,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 que mi esposa sirva a otro, que otros hombres se acuesten con ella.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Porque eso sería una maldad, un pecado que merece castigo,
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 porque este pecado es como un fuego que lleva a la destrucción, destruyendo todo lo que tengo.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 “Si me negara a escuchar a mis siervos o siervas cuando me trajeran sus quejas,
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 ¿qué haría cuando Dios viniera a juzgarme? ¿Cómo respondería si me investigara?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 ¿Acaso el mismo Dios no nos hizo a todos?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 ¿Me he negado a dar a los pobres lo que necesitaban, o he hecho desesperar a las viudas?
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 ¿Acaso he comido yo solo un trozo de pan? ¿No he compartido siempre mi comida con los huérfanos?
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 Desde que era joven fui padre de los huérfanos y cuidé de las viudas.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Si alguna vez veía a alguien necesitado de ropa, a los pobres sin nada que ponerse,
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 siempre me agradecían la ropa de lana que los mantenía calientes.
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 “Si levantaba la mano para golpear a un huérfano, seguro de que si llegaba a los tribunales los jueces estarían de mi parte,
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 entonces que mi hombro sea arrancado de su articulación, que mi brazo sea arrancado de su cavidad.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Como me aterra el castigo que Dios me tiene reservado, y debido a su majestad, nunca podría hacer esto.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 “¿He puesto mi confianza en el oro, llamando al oro fino ‘mi seguridad’?
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 ¿Me he deleitado en ser rico, feliz por todas mis riquezas que había ganado?
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 ¿He mirado el sol brillando tan intensamente o la luna moviéndose con majestuosidad por el cielo
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 y he tenido la tentación de adorarlos secretamente besando mi mano ante ellos como señal de devoción?
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 Esto también sería un pecado que merece castigo porque significaría que he negado a Dios en lo alto.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 “¿Alguna vez me he alegrado cuando el desastre destruyó a los que me odiaban, o he celebrado cuando el mal los derribó?
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Nunca he permitido que mi boca pecara echando una maldición sobre la vida de alguien.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 ¿No ha preguntado mi familia: ‘¿Hay alguien que no haya comido todo lo que quería de su comida?’
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Nunca he dejado dormir a extraños en la calle; he abierto mis puertas a los viajeros.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 ¿He ocultado mis pecados a los demás, escondiendo mi maldad en lo más profundo de mí?
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 ¿Tenía miedo de lo que pensaran los demás, del desprecio que me hicieran las familias, y por eso me callaba y no salía?
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 “¿Por qué nadie escucha lo que digo? Firmo con mi nombre para avalar todo lo que he dicho. Que el Todopoderoso me responda. Que mi acusador escriba de qué me acusa.
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Yo los pondría en alto; Los llevaría en mi cabeza como una corona.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Le explicaría todo lo que había hecho; mantendría la cabeza alta ante él.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 “Si mi tierra ha gritado contra mí; si sus surcos han llorado por mí;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 si he tomado sus cosechas sin pago o si he causado daño a los agricultores;
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 entonces que crezcan espinas en lugar de trigo, y cizaña en lugar de cebada”. Las palabras de Job se terminan.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >