< Psalmi 7 >

1 Pesem meševita Davidova, katero je pel Gospodu na besede Kusa Benjaminca. Gospod, Bog moj, k tebi pribegam; reši me vseh preganjalcev mojih in oprosti me.
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 Da ne zgrabi kakor lev duše moje in raztrga, ko ni pomočnika.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Gospod, Bog moj, ako sem storil tisto, ako je krivica na rokah mojih:
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 Ako sem storil hudo v miru živečemu z menoj, ki sem mu rad pomagal, kateri me je zatiral po krivem:
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 Preganja naj sovražnik dušo mojo in dohiti ter potepta na tleh življenje moje; in storí naj, da v prahu biva slava moja.
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Vstani, Gospod, v jezi svoji; dvigni se silno razkačen proti njim, ki me zatirajo; in čuj nad menoj, sodbo si zapovedal.
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Torej narodov zbor naj te obdá in nad njim vrni se v višavo.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Gospod sodi ljudstva; sodi me, Gospod, po pravičnosti moji in po nedolžnosti moji razsodi zame.
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Propade naj, prosim, zlo krivičnih, in pravičnega utrdi; kakor preiskuješ srca in obisti, Bog pravični.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Ščit moj je v Bogu, ki daje blaginjo pravičnim v srci,
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 V Bogu, ki je pravičnemu bramba in Bogu mogočnem, ki se srdi vsak dan.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ako se ne izpreobrne krivični, nabrusi svoj meč; lok svoj je napél in pomeril vanj.
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Pomeril je vanj smrtno orožje; pušice svoje zgrabi zoper divjajoče.
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Glej, rodil bode ničemurnost; kakor je spočel nadlogo, tako bode rodil laž.
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Vodnjak je kopal in izglobal ga; vanj je planil, v jami opravljat delo svoje.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Povrne se nadloga njegova na glavo njegovo in nad téme njegovo pride njegova krivica.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Slaviti hočem Gospoda po pravici njegovi in prepeval bodem imenu Gospoda najvišjega.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Psalmi 7 >