< Kološanom 3 >

1 Če ste bili torej vred zbujeni s Kristusom, iščite, kar je gori, kjer sedí Kristus na desnici Božji.
Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
2 V mislih imejte, kar je gori, ne kar je na zemlji;
Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
3 Kajti umrli ste, in življenje vaše je skrito s Kristusom v Bogu;
Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
4 Kader se prikaže Kristus, življenje naše, tedaj se prikažete tudi vi v slavi z njim.
Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
5 Morite torej ude svoje zemeljske, kurbarijo, nečistost, strast, hudo poželenje in lakomnost, katera je malikovanje;
Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
6 Po čemer prihaja jeza Božja nad nepokorščine sinove,
Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
7 Med katerimi ste tudi vi živeli nekdaj, ko ste bivali med njimi;
Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
8 Sedaj pa odložite tudi vi vse, jezo, srd, hudobnost, obrekovanje, nesramno besedovanje iz svojih ust.
Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
9 Ne lagajte med seboj, slecite starega človeka z dejanji njegovimi,
Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
10 In oblecite novega, ponovljenega v spoznanje po podobi njega, ki ga je vstvaril;
ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
11 Kjer ni Grka in Juda, obreze in neobreze, tujca, Scita, hlapca, svobodnjaka; nego vse in v vseh Kristus.
Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
12 Oblecite torej, ker ste izvoljeni in ljubljeni sveti Božji, milosrčnost, blagovoljnost, ponižnost, krotkost, potrpežljivost;
Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
13 Da se prenašate med seboj, in si odpuščate, če ima kdo tožbo do koga, kakor je tudi Kristus odpustil vam, tako tudi vi;
Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
14 Poleg vsega tega pa ljubezen, katera je popolnosti vez.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
15 In mir Božji naj vlada v srcih vaših, v katerega ste bili tudi poklicani v enem telesu; in hvaležni bodite!
Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
16 Beseda Kristusova prebivaj v vas obilo, v vsej modrosti; učite in opominjajte se med seboj s psalmi in hvalospevi in pesmami duhovnimi, v milosti pójte v srci svojem Gospodu.
Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
17 In vse, kar počenjate v besedi in dejanji, vse v imenu Gospoda Jezusa, zahvaljujoč se Bogu in očetu po njem.
Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
18 Žene, bodite pokorne svojim možem, kakor se spobodi v Gospodu.
Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Možje, ljubite žene svoje in ne hudujte se nad njimi.
Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Otroci, bodite poslušni roditeljem v vsem, kajti to je po volji Gospodu.
Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Očetje, ne dražite otrók svojih, da ne bodo malosrčni.
Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Hlapci, bodite poslušni v vsem gospodom po mesu, ne po okoslužnosti kakor ljudem ugajajoč, nego v preprostosti srca, boječ se Boga.
Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
23 In vse kar storite, delajte iz duše, kakor Gospodu, in ne ljudém;
Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
24 Vedóč, da od Kristusa dobóte zato povračilo dedščine; kajti Gospodu Kristusu hlapčujete;
Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
25 Krivični pa bode prejel, kar je krivičnega storil; in ni ga licegledja.
Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

< Kološanom 3 >