< Luka 5 >

1 In pripetilo se je, medtem ko je množica pritiskala nanj, da sliši Božjo besedo, [da] je stal ob Genezareškem jezeru
Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
2 in zagledal dve ladji, pripravljeni pri jezeru, toda ribiči so odšli iz njiju ter izpirali svoje mreže.
Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
3 In vstopil je v eno izmed ladij, ki je bila Simonova in ga prosil, da bi odrinil malce proč od kopnega. In usedel se je ter iz ladje učil množico.
Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
4 Torej, ko je prenehal govoriti, je rekel Simonu: »Kreni na globoko in spusti dol svoje mreže za vleko.«
Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
5 Simon pa mu odgovori in reče: »Učitelj, celó noč smo garali, pa nismo nič ujeli. Vendar bom na tvojo besedo to mrežo spustil dol.«
Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
6 In ko so to storili, so zajeli veliko množino rib in njihova mreža se je pretrgala.
Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
7 In dali so znamenje svojim družabnikom, ki so bili na drugi ladji, da naj pridejo ter jim pomagajo. In prišli so ter napolnili obe ladji, tako da sta se začeli potapljati.
Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
8 Ko je Simon Peter to videl, je pri Jezusovih kolenih padel dol, rekoč: »Odidi od mene, oh Gospod, kajti grešen človek sem.«
Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
9 Kajti nad ulovom rib, ki so jih zajeli, je bil osupel on in vsi ti, ki so bili z njim;
Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
10 in tako sta bila tudi Jakob in Janez, Zebedejeva sinova, ki sta bila Simonova družabnika. In Jezus je Simonu rekel: »Ne boj se, odslej boš lovil ljudi.«
chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
11 In ko so svoji ladji pripeljali do kopnega, so vse zapustili in mu sledili.
Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
12 In pripetilo se je, ko je bil v nekem mestu, [da] zagleda človeka polnega gobavosti. Ko je [le-ta] zagledal Jezusa, je padel na svoj obraz ter ga rotil, rekoč: »Gospod, če hočeš, me lahko očistiš.«
Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
13 In iztegnil je svojo roko ter se ga dotaknil, rekoč: »Hočem, bodi čist.« In gobavost je takoj odšla od njega.
Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
14 In naročil mu je, da ne pove nobenemu človeku: »Temveč pojdi in se pokaži duhovniku ter daruj za svoje očiščenje glede na Mojzesovo zapoved, njim v pričevanje.«
Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
15 Toda beseda o njem je toliko bolj na veliko šla naokoli in velike množice so prišle skupaj, da poslušajo in da bi bile po njem ozdravljene svojih slabotnosti.
Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
16 On pa se je umaknil v divjino in molil.
Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
17 In pripetilo se je na določeni dan, medtem ko je učil, da so bili tam, sedeči poleg, farizeji in učeni možje postave, ki so prišli iz vsakega mesta Galileje, Judeje in Jeruzalema. In Gospodova moč je bila prisotna, da jih ozdravi.
Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
18 In glej, možje so prinesli na postelji človeka, ki je bil prevzet s paralizo in iskali so načine, da ga prinesejo noter in da ga položijo predenj.
Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
19 Ko pa zaradi množice niso mogli najti, po kateri poti bi ga lahko prinesli noter, so odšli na hišno streho in ga z njegovim ležiščem vred spustili navzdol skozi strešno kritino v sredo pred Jezusa.
Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
20 In ko je videl njihovo vero, mu je rekel: »Človek, tvoji grehi so ti odpuščeni.«
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
21 In pisarji in farizeji so začeli premišljevati, rekoč: »Kdo je ta, ki govori bogokletja? Kdo lahko odpušča grehe razen samo Bog?«
Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
22 Toda ko je Jezus zaznal njihove misli, jim je odgovoril in rekel: »Kaj razmišljate v svojih srcih?
Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
23 Ali je lažje reči: ›Tvoji grehi naj ti bodo odpuščeni‹ ali reči: ›Dvigni se in hôdi?‹
Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
24 Toda da boste lahko vedeli, da ima Sin človekov na zemlji oblast odpuščati grehe, « (je rekel bolnemu zaradi paralize) »jaz ti pravim: ›Vstani in vzemi svoje ležišče in pojdi v svojo hišo.‹«
Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
25 In ta je pred njimi takoj vstal ter pobral to, na čemer je ležal in odšel k svoji lastni hiši, proslavljajoč Boga.
Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
26 In vsi so bili osupli in slavili Boga in izpolnjeni so bili s strahom, rekoč: »Danes smo videli čudne stvari.«
Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
27 Po teh stvareh pa je odšel dalje in zagledal davkarja, imenovanega Levi, ki je sedel pri kraju plačevanja davkov in mu rekel: »Sledi mi.«
Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
28 In ta je pustil vse, vstal ter mu sledil.
Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
29 In Levi mu je v svoji lastni hiši pripravil veliko praznovanje; in bila je velika skupina davkarjev in drugih, ki so se z njimi usedli.
Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
30 Toda njihovi pisarji in farizeji so godrnjali zoper njegove učence, rekoč: »Zakaj jeste in pijete z davkarji in grešniki?«
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
31 In Jezus jim odgovori ter reče: »Tisti, ki so zdravi, ne potrebujejo zdravnika, temveč tisti, ki so bolni.
Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
32 Nisem prišel klicat pravičnih, temveč grešnike h kesanju.«
Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
33 In rekli so mu: »Zakaj se Janezovi učenci pogosto postijo in opravljajo molitve in enako učenci farizejev, tvoji pa jedo in pijejo?«
Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
34 Rekel jim je: »Ali lahko primorate otroke svatovske sobe, da se postijo, medtem ko je z njimi ženin?
Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
35 Toda prišli bodo dnevi, ko bo ženin odvzet od njih in tedaj, v tistih dneh, se bodo postili.«
Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
36 In povedal jim je tudi prispodobo: »Nihče ne polaga koščka iz nove obleke na staro; če drugače, potem nov dela raztrganino in tudi košček, ki je bil odvzet iz nove, se ne ujema s staro.
Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
37 In novega vina nihče ne vliva v stare mehove, sicer bo novo vino mehove razgnalo in bo izlito in mehovi bodo propadli.
Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
38 Toda novo vino mora biti vlito v nove mehove in oboje je ohranjeno.
Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
39 Prav tako nihče, ki je pil staro vino, noče nemudoma novega, kajti pravi: ›Staro je boljše.‹«
Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”

< Luka 5 >