< Job 16 >

1 Potem je Job odgovoril in rekel:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 »Slišal sem mnoge takšne stvari. Vi vsi ste bedni tolažniki.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Mar bodo besede ničnosti imele konec? Ali kaj te opogumlja, da odgovarjaš?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Tudi jaz bi lahko govoril, kakor delate vi. Če bi bila vaša duša namesto moje duše, bi lahko kopičil besede zoper vas in z glavo zmajeval nad vami.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Toda jaz bi vas želel okrepiti s svojimi usti in premikanje mojih ustnic bi omililo vašo žalost.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Čeprav govorim, moja žalost ni zmanjšana in čeprav potrpim, koliko sem olajšan?
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Toda sedaj me je naredil izmučenega. Vso mojo skupino si naredil zapuščeno.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Napolnil si me z gubami, ki so priča zoper mene. Moja pustost vstaja v meni in pričuje v moj obraz.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Trga me v svojem besu ta, ki me sovraži. Nad menoj škripa s svojimi zobmi. Moj sovražnik svoje oči ostri nad menoj.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 S svojimi usti so zevali vame. Grajalno so me udarili na lice. Skupaj so se zbrali zoper mene.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Bog me je izročil brezbožnim in me predal v roke zlobnih.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Bil sem sproščen, toda razlomil me je. Prijel me je tudi za moj vrat in me stresel na koščke in me postavil za svoje znamenje.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Njegovi lokostrelci so me obdali naokoli, on mojo notranjost cepi narazen in ne prizanaša; moj žolč izliva na tla.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Lomi me z vrzeljo nad vrzeljo, nadme teče kakor velikan.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Sešil sem vrečevino na svoji koži in svoj rog omadeževal v prahu.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Moj obraz je zapacan od joka in na mojih vekah je smrtna senca,
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 ne zaradi kakršnekoli nepravičnosti na mojih rokah. Tudi moja molitev je čista.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 Oh zemlja, ne pokrij moje krvi in naj moj jok nima prostora.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Tudi sedaj, glej, moja priča je v nebesih in moje pričevanje je na višini.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Moji prijatelji me zasmehujejo, toda moje oko izliva solze k Bogu.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 Oh, da bi se nekdo lahko potegoval za človeka pri Bogu, kakor se človek poteguje za svojega bližnjega!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Ko pride nekaj let, potem bom šel pot, od koder se ne bom vrnil.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >