< Ezekiel 22 >

1 Poleg tega je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anandiyankhula nati:
2 »Torej, človeški sin, ali boš sodil, ali boš sodil krvoločno mesto? Da, pokazal mu boš vse njegove ogabnosti.
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 Potem reci: ›Tako govori Gospod Bog: ›Mesto v svoji sredi preliva kri, da lahko pride njegov čas in zoper sebe izdeluje malike, da se omadežuje.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 Postalo si krivo v svoji krvi, ki si jo prelilo; in omadeževalo si se s svojimi maliki, ki si jih naredilo; in svojim dnevom si povzročilo, da so se približali in prišlo si celó k svojim letom. Zato sem te naredil za grajo poganom in zasmeh vsem deželam.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 Tisti, ki so blizu in tisti, ki so daleč od tebe, te bodo zasmehovali, ki so neslavni in precej nadležni.
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Glej, Izraelovi princi, vsak je bil v tebi k njihovi moči, da preliva kri.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 V tebi so prezirali očeta in mater. V tvoji sredi so z zatiranjem postopali s tujcem. V tebi so nadlegovali osirotelega in vdovo.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 Preziralo si moje svete stvari in oskrunilo moje šabate.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 V tebi so ljudje, ki prenašajo govorice, da prelijejo kri; in v tebi jedo po gorah. V tvoji sredi zagrešujejo nespodobnost.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 V tebi so odkrili nagoto svojih očetov. V tebi so ponižali tisto, ki je bila oddvojena zaradi oskrunitve.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 In nekdo je zagrešil ogabnost z ženo svojega soseda; in drugi je opolzko omadeževal svojo snaho; in drugi je v tebi ponižal svojo sestro, hčer svojega očeta.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 V tebi so jemali darila, da prelijejo kri. Jemalo si obresti in donos in z izsiljevanjem si lakomno pridobivalo od svojih sosedov in si me pozabilo, ‹ govori Gospod Bog.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 ›Glej, zato sem udaril svojo roko ob tvoj nepošten dobiček, ki si ga naredilo in pri tvoji krvi, ki je bila v tvoji sredi.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Ali tvoje srce lahko prenese, ali so tvoje roke lahko močne v dneh, ko bom obračunal s teboj? Jaz, Gospod sem to govoril in bom to storil.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 In razkropil te bom med pogane in te razpršil v dežele in iz tebe použil tvojo umazanost.
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 In vzelo boš svojo dediščino v sebi, pred očmi poganov in vedelo boš, da jaz sem Gospod.‹«
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 In k meni je prišla Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anandiyankhula nati:
18 »Človeški sin, Izraelova hiša mi je postala žlindra. Vsi so bron, kositer, železo in svinec v sredi talilne peči; so celó srebrova žlindra.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 Zato tako govori Gospod Bog: ›Ker ste vsi postali žlindra, glejte, zato vas bom zbral v sredi [prestolnice] Jeruzalem.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 Kakor oni zbirajo srebro in bron in železo in svinec in kositer v sredi talilne peči, da nanjo pihajo ogenj, da to raztalijo; tako vas bom jaz zbral v svoji jezi in svoji razjarjenosti in vas bom pustil tam in vas raztalil.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 Da, zbral vas bom in pihal nad vas v ognju svojega besa in vi boste raztaljeni v njeni sredi.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 Kakor je srebro raztaljeno v sredi talilne peči, tako boste raztaljeni v njeni sredi in spoznali boste, da sem jaz, Gospod, nad vas izlil svojo razjarjenost.‹«
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 In k meni je prišla Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 »Človeški sin, reci ji: ›Ti si dežela, ki ni očiščena niti ni nanjo deževalo na dan ogorčenja.
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 Tam je zarota njenih prerokov v njeni sredi, podobna rjovenju leva, željnega plena. Požrli so duše, vzeli so zaklad in dragocene stvari; v njeni sredi so naredili mnogo vdov.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Njeni duhovniki so prekršili mojo postavo in oskrunili moje svete stvari. Niso pokazali nobene razlike med svetim in oskrunjenim niti niso pokazali razlike med nečistim in čistim in svoje oči so skrili pred mojimi šabati in jaz sem med njimi oskrunjen.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Njeni princi v njeni sredi so podobni volkovom, željnim plena, da prelijejo kri in da uničijo duše, da pridobijo nepošten dobiček.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 In njeni preroki so jih ometali z neutrjeno malto, gledoč ničnost in vedeževali so jim laži, rekoč: ›Tako govori Gospod Bog, ‹ ko Gospod ni govoril.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 Ljudstvo dežele je uporabljalo zatiranje in izvajalo rop in jezilo revne in pomoči potrebne; da, krivično so zatirali tujca.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 In iskal sem človeka med njimi, ki bi naredil ograjo in stal v razpoki pred menoj za deželo, da je ne bi uničil, toda nikogar nisem našel.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 Zato sem nadnje izlil svoje ogorčenje; použil sem jih z ognjem svojega besa. Njihovo lastno pot sem poplačal na njihovih glavah, ‹ govori Gospod Bog.‹«
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 22 >