< Числа 16 >

1 И глагола Корей, сын Иссаара сына Каафа сына Левиина, и Дафан и Авирон, сынове Елиавли, и Авнан сын Фалефа сына Рувимля:
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2 и восташа на Моисеа, и мужи сынов Израилевых двести и пятьдесят началницы сонма, сигклитики совета и мужи именити.
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
3 Совосташа на Моисеа и Аарона и реша к ним: довлеет вам, яко весь сонм вси святи, и в них Господь: и чесо ради востаете на сонм Господнь?
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
4 И слышав Моисей, паде ниц.
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
5 И глагола к Корею и ко всему сонму его, глаголя: согляда и позна Господь сущих Его и святых, и приведе к Себе: и ихже не избра Себе, не приведе к себе:
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
6 сие сотворите: возмите себе сами кадилники, Корей и весь сонм его,
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7 и вложите огнь в ня, и вложите в ня фимиам пред Господем утре: и будет муж, егоже аще изберет Господь, сей свят: да довлеют вам сынове Левиины.
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
8 И рече Моисей Корею: послушайте мене, сынове Левиини:
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9 еда мало есть сие вам, яко отлучи вас Бог от сонма Израилева и приведе вас к Себе служити службы в скинии Господни и стояти пред сонмом Господним, еже служити им?
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
10 И приведе тя и всю братию твою, сыны Левиины с тобою, и просите священствовати?
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
11 Тако ты и весь сонм твой собравшийся на Бога: и Аарон кто есть, яко ропщете нань?
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
12 И посла Моисей призвати Дафана и Авирона, сыны Елиавли. И реша: не идем:
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
13 еда мало се, яко извел еси ны из земли кипящия млеком и медом, еже погубити нас в пустыни, яко владееши нами? Князь еси:
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
14 и ты ли в землю кипящую медом и млеком ввел еси нас и дал еси нам часть села и винограда? Очи человек тех изткнул еси: не идем.
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
15 И отягча Моисей гневом зело и рече к Господу: не внемли на жертву их: ни единаго похотения от них приях, ниже озлобих кого от них.
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
16 И рече Моисей к Корею: освяти сонм твой, и будите готови пред Господа ты и Аарон и они заутра:
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
17 и возмите кийждо кадилник свой, и возложите на ня фимиам, и принесите пред Господа кийждо кадилник свой, двести и пятьдесят кадилников, и ты и Аарон кийждо кадилник свой.
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
18 И взяша кийждо свой кадилник, и возложиша на ня огнь, и вложиша в ня фимиам, и сташа пред дверми скинии свидения Моисей и Аарон.
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 И собра на ня Корей весь сонм свой пред дверми скинии свидения: и явися слава Господня всему сонму.
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
20 И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
21 отступите кийждо от среды сонма сего, и потреблю Я абие.
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
22 И падоста на лица своя и рекоста: Боже, Боже духов и всякия плоти: аще человек един согреши, на весь ли сонм гнев Господнь?
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
23 И рече Господь к Моисею, глаголя:
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
24 рцы сонму, глаголя: отступите окрест от сонма Кореева и Дафаня и Авироня.
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
25 И воста Моисей, и иде к Дафану и Авирону: и идоша с ним вси старцы Израилтестии.
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
26 И рече к сонму, глаголя: отступите от кущ человек жестокосердых сих, и не прикоснитеся ко всем, елика суть им, да не погибнете купно во всем гресе их.
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
27 И отступиша от кущ Кореа и Дафана и Авирона окрест: Дафан же и Авирон изыдоста и стаста пред дверми кущ своих, и жены их, и дети их и имение их.
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
28 И рече Моисей: в сем познаете, яко Господь посла мя сотворити вся дела сия, яко не от себе (аз творю сия):
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
29 аще смертию всех людий умрут сии, и аще по присещению всех человек посещение будет их, то не Господь посла мене:
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
30 но явно покажет Господь, и отверзши земля уста своя пожрет я и домы их, и кущы их и вся, елика суть их, и снидут живи во ад, и уведите, яко разгневаша человецы сии Господа. (Sheol h7585)
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
31 Егда же преста глаголя вся словеса сия, разседеся земля под ногами их:
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
32 и разверзеся земля, и пожре я и домы их, и вся люди сущыя с Кореом, и скоты их:
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
33 и снидоша тии, и вся, елика суть их, живи во ад, и покры их земля, и погибоша от среды сонма: (Sheol h7585)
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
34 и весь Израиль, и иже окрест их, отбегоша от вопля их, зане рекоша, глаголюще: да не пожрет нас земля.
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
35 И огнь изыде от Господа и пояде двести и пятьдесят мужей принесших фимиам.
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
36 И рече Господь к Моисею.
Yehova anawuza Mose kuti,
37 И ко Елеазару сыну Ааронову жерцу: соберите кадилники медяныя от среды изгоревших, и огнь чуждий сей разсыплите тамо, яко освятишася кадилницы грешных сих в душах их:
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38 и сотворите я дщицы кованы, обложение у олтаря, яко принесошася пред Господа и освятишася, и быша в знамение сыном Израилевым.
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
39 И взя Елеазар сын Аарона жерца кадилники медяныя, елики принесоша изгоревшии, и обложиша я во обложение олтаря,
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
40 в память сыном Израилевым яко да никтоже приидет иноплеменник, иже несть от семене Аароня, еже возложити фимиам пред Господем, и да не будет, якоже Корей и советницы его, якоже глагола ему Господь рукою Моисеовою.
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
41 И возропташа сынове Израилтестии на утрие на Моисеа и Аарона, глаголюще: вы избисте люди Господни.
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
42 И бысть егда нападе сонм на Моисеа и Аарона, и устремишася к скинии свидения:
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
43 и покры оную облак, и явися слава Господня: и вниде Моисей и Аарон пред скинию свидения.
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44 И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
45 уступите от среды сонма сего и потреблю я единицею. И падоста на лица своя.
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
46 И рече Моисей ко Аарону: возми кадилник, и вложи в него огнь от олтаря, и возложи нань фимиам, и понеси скоро в полк, и помолися о них: изыде бо гнев от лица Господня, и нача губити люди.
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
47 И взя Аарон, якоже глагола ему Моисей, и тече в сонм, уже бо начася пагуба в людех: и возложи фимиам, и помолися о людех:
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
48 и ста между мертвыми и живыми, и преста пагуба.
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
49 И бысть умерших в пагубе четыренадесять тысящ и седмь сот кроме умерших Кореа ради.
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
50 И возвратися Аарон к Моисею, к дверем скинии свидения, и преста пагуба.
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

< Числа 16 >