< От Матфея святое благовествование 23 >

1 Тогда Иисус глагола к народом и учеником Своим,
Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake:
2 глаголя: на Моисеове седалищи седоша книжницы и фарисее:
“Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose.
3 вся убо, елика аще рекут вам блюсти, соблюдайте и творите: по делом же их не творите: глаголют бо, и не творят:
Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa.
4 связуют бо бремена тяжка и бедне носима, и возлагают на плеща человеческа, перстом же своим не хотят двигнути их.
Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.
5 Вся же дела своя творят, да видими будут человеки: разширяют же хранилища своя и величают воскрилия риз своих:
“Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo.
6 любят же преждевозлегания на вечерях, и преждеседания на сонмищих,
Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge.
7 и целования на торжищих, и зватися от человек: учителю, учителю.
Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’
8 Вы же не нарицайтеся учителие: един бо есть ваш Учитель, Христос: вси же вы братия есте:
“Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale.
9 и отца не зовите себе на земли: един бо есть Отец ваш, Иже на небесех:
Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba.
10 ниже нарицайтеся наставницы: един бо есть Наставник ваш, Христос.
Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu.
11 Болий же в вас да будет вам слуга:
Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani.
12 иже бо вознесется, смирится: и смиряяйся вознесется.
Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.
13 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко затворяете Царствие Небесное пред человеки: вы бо не входите, ни входящих оставляете внити.
“Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe.
14 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко снедаете домы вдовиц, и виною далече молитвы творяще: сего ради лишшее приимете осуждение.
Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.
15 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко преходите море и сушу, сотворити единаго пришелца: и егда будет, творите его сына геенны сугубейша вас. (Geenna g1067)
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna g1067)
16 Горе вам, вожди слепии, глаголющии: иже аще кленется церковию, ничесоже есть: а иже кленется златом церковным, должен есть.
“Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
17 Буи и слепии, что бо более есть, злато ли, или церковь, святящая злато?
Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo?
18 И: иже аще кленется олтарем, ничесоже есть: а иже кленется даром, иже верху его, должен есть.
Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
19 Буи и слепии, что бо более, дар ли, или олтарь, святяй дар?
Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo?
20 Иже убо кленется олтарем, кленется им и сущим верху его:
Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo.
21 и иже кленется церковию, кленется ею и Живущим в ней:
Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo.
22 и кленыйся небесем кленется Престолом Божиим и Седящим на нем.
Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.
23 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко одесятствуете мятву и копр и кимин, и остависте вящшая закона, суд и милость и веру: сия (же) подобаше творити, и онех не оставляти.
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo.
24 Вожди слепии, оцеждающии комары, велблуды же пожирающе.
Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.
25 Горе вам, книжницы и фарисее лицемери, яко очищаете внешнее сткляницы и блюда, внутрьуду же суть полни хищения и неправды:
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa.
26 фарисее слепый, очисти прежде внутреннее сткляницы и блюда, да будет и внешнее има чисто.
Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.
27 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко подобитеся гробом повапленым, иже внеуду убо являются красны, внутрьуду же полни суть костей мертвых и всякия нечистоты:
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse.
28 тако и вы, внеуду убо являетеся человеком праведни, внутрьуду же есте полни лицемерия и беззакония.
Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.
29 Горе вам, книжницы и фарисее, лицемери, яко зиждете гробы пророческия, и красите раки праведных,
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama.
30 и глаголете: аще быхом были во дни отец наших, не быхом убо общницы им были в крови пророк:
Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’
31 темже сами свидетелствуете себе, яко сынове есте избивших пророки:
Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.
32 и вы исполните меру отец ваших.
Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!
33 Змия, порождения ехиднова, како убежите от суда (огня) геенскаго? (Geenna g1067)
“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna g1067)
34 Сего ради, се, Аз послю к вам пророки и премудры и книжники: и от них убиете и распнете, и от них биете на сонмищих ваших, и изженете от града во град:
Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina.
35 яко да приидет на вы всяка кровь праведна, проливаемая на земли, от крове Авеля праведнаго до крове Захарии сына Варахиина, егоже убисте между церковию и олтарем.
Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu.
36 Аминь глаголю вам: (яко) приидут вся сия на род сей.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.
37 Иерусалиме, Иерусалиме, избивый пророки и камением побиваяй посланныя к тебе, колькраты восхотех собрати чада твоя, якоже собирает кокош птенцы своя под криле, и не восхотесте?
“Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune.
38 Се, оставляется вам дом ваш пуст.
Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja.
39 Глаголю бо вам: (яко) не имате Мене видети отселе, дондеже речете: благословен Грядый во имя Господне.
Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’”

< От Матфея святое благовествование 23 >